< 1 Tessalonikerne 1 >

1 Paulus og Silvanus og Timoteus - til tessalonikernes menighet i Gud Fader og den Herre Jesus Kristus: Nåde være med eder og fred!
Paulo, Silivano ndi Timoteyo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu.
2 Vi takker alltid Gud for eder alle når vi kommer eder i hu i våre bønner,
Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu.
3 idet vi uavlatelig minnes eders virksomhet i troen og arbeid i kjærligheten og tålmod i håpet på vår Herre Jesus Kristus for vår Guds og Faders åsyn,
Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
4 da vi er visse på at I er utvalgt, brødre, I som er elsket av Gud.
Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani,
5 For vårt evangelium kom ikke til eder bare i ord, men og i kraft og i den Hellige Ånd og i stor fullvisshet, likesom I jo vet hvorledes vi var iblandt eder for eders skyld,
chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni.
6 og I blev efterfølgere av oss og av Herren, idet I tok imot ordet under megen trengsel med glede i den Hellige Ånd,
Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera.
7 så I er blitt et forbillede for alle de troende i Makedonia og Akaia.
Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya.
8 For fra eder har Herrens ord lydt ut; ikke bare i Makedonia og Akaia, men allesteds er eders tro på Gud kommet ut, så vi ikke trenger til å tale noget om det;
Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu,
9 for selv forteller de om oss hvad inngang vi fikk hos eder, og hvorledes I vendte eder til Gud fra avgudene, for å tjene den levende og sanne Gud
pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona.
10 og vente på hans Sønn fra himlene som han opvakte fra de døde, Jesus, han som frir oss fra den kommende vrede.
Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.

< 1 Tessalonikerne 1 >