< 1 Kongebok 3 >

1 Og Salomo inngikk svogerskap med Farao, Egyptens konge; han tok Faraos datter til ekte og førte henne inn i Davids stad inntil han blev ferdig med å bygge både sitt eget hus og Herrens hus og muren rundt omkring Jerusalem.
Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
2 Folket ofret dengang bare på haugene; for på den tid var det ennu ikke bygget noget hus for Herrens navn.
Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
3 Salomo elsket Herren, så han fulgte sin far Davids forskrifter; dog ofret han på haugene og brente røkelse der.
Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
4 Og kongen drog til Gibeon for å ofre der; for der var den ypperste offerhaug. Tusen brennoffer ofret Salomo på alteret der.
Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
5 I Gibeon åpenbarte Herren sig for Salomo i en drøm om natten; Gud sa: Bed om det du vil jeg skal gi dig!
Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
6 Salomo svarte: Du har vist stor miskunnhet mot din tjener David, min far, efterdi han vandret for ditt åsyn i sannhet og i rettferdighet og i hjertets opriktighet mot dig, og denne store miskunnhet vedblev du stadig å vise ham og gav ham en sønn som skulde sitte på hans trone, således som det er idag.
Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
7 Nu har du da, Herre min Gud, gjort din tjener til konge i min far Davids sted; men jeg er bare en ungdom og vet ikke hvorledes jeg skal bære mig at i ett og alt.
“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
8 Og din tjener står her midt iblandt ditt folk, det som du har utvalgt, et folk som er så stort at det ikke kan regnes eller telles, så stort er det.
Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
9 Så gi da din tjener et hørsomt hjerte til å dømme ditt folk, til å skille mellem godt og ondt! For hvem kunde ellers dømme dette ditt folk som er så tallrikt?
Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
10 Herren syntes godt om at Salomo hadde bedt om denne ting.
Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
11 Og Gud sa til ham: Efterdi du har bedt om denne ting og ikke bedt om et langt liv og ikke bedt om rikdom og heller ikke om dine fienders død, men har bedt om forstand til å akte på hvad rett er,
Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
12 så vil jeg gjøre som du beder: Jeg vil gi dig et vist og forstandig hjerte, så det ikke har vært din like før og ikke vil komme din like efter dig.
Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
13 Og det du ikke har bedt om, vil jeg og gi dig, både rikdom og ære, så det ikke skal være din like blandt kongene alle dine dager.
Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
14 Og dersom du vil vandre på mine veier, så du holder mine lover og mine bud, som din far David gjorde, så vil jeg gi dig et langt liv.
Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
15 Da våknet Salomo, og han skjønte at det var en drøm. Og da han kom til Jerusalem, trådte han frem for Herrens pakts-ark og ofret brennoffer og bar frem takkoffer og gjorde et gjestebud for alle sine tjenere.
Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
16 På den tid kom det to skjøger og trådte frem for kongen.
Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
17 Og den ene kvinne sa: Hør på mig, herre! Jeg og denne kvinne bodde i samme hus, og jeg fødte et barn i huset hos henne.
Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
18 Og den tredje dag efterat jeg hadde født, fødte også denne kvinne et barn. Der var vi nu sammen; det var ingen fremmed hos oss i huset; bare vi to var i huset.
Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
19 Om natten døde sønnen til denne kvinne fordi hun hadde ligget på ham;
“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
20 og hun stod op midt om natten og tok min sønn fra min side, mens din tjenerinne sov, og hun la ham ved sin barm, og sin egen sønn som var død, la hun ved min barm.
Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
21 Da jeg så stod op om morgenen for å gi min sønn die, fikk jeg se at han var død; men da jeg om morgenen så nøiere på ham, da var det ikke min sønn, den som jeg hadde født.
Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
22 Da sa den andre kvinne: Nei, den som lever, er min sønn, og den som er død, er din. Men den første sa: Nei, den som er død, er din sønn, og den som lever, er min. Således talte de mens de stod for kongen.
Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
23 Da sa kongen: Den ene sier: Denne som lever, er min sønn, og den som er død, er din. Og den andre sier: Nei, den som er død, er din sønn, og den som lever, er min.
Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
24 Så sa kongen: Hent mig et sverd! Og de kom med et sverd og bar det frem for kongen.
Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
25 Da sa kongen: Hugg det levende barn i to stykker og gi den ene halvdel til den ene og den andre halvdel til den andre!
Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
26 Da sa den kvinne som var mor til det levende barn, til kongen - for hennes hjerte brente for hennes barn - hun sa: Hør på mig, herre! Gi henne det levende barn og drep det for all ting ikke! Men den andre sa: Hverken jeg eller du skal ha det; hugg bare til!
Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
27 Da tok kongen til orde og sa: Gi henne det levende barn og drep det ikke! Hun er dets mor.
Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
28 Hele Israel fikk høre om den dom kongen hadde felt, og de hadde ærefrykt for kongen; for de så at Guds visdom var i hans hjerte, så at han dømte rett.
Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.

< 1 Kongebok 3 >