< 1 Kongebok 1 >

1 Nu var kong David gammel og høit til års, og de dekket ham til med tepper, men han kunde ikke bli varm.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Da sa hans tjenere til ham: En skulde lete efter en ung pike for min herre kongen, en jomfru som kan stelle for kongen og pleie ham og ligge i din favn, så min herre kongen blir varm.
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Så lette de i hele Israels land efter en vakker pike, og de fant Abisag fra Sunem og førte henne til kongen.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Det var en meget vakker pike; hun pleide kongen og tjente ham, men kongen hadde ikke omgang med henne.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 Men Adonja, sønn til Haggit, gjorde sig høie tanker og sa: Jeg vil være konge. Og han fikk sig vogner og hestfolk og femti mann som løp foran ham.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 Hans far hadde aldri i hans liv talt hårdt til ham og sagt: Hvorfor har du gjort dette? Han var og meget fager, og han var født næst efter Absalom.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 Han samrådde sig med Joab, Serujas sønn, og med presten Abjatar, og de holdt med Adonja og hjalp ham.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Men presten Sadok og Benaja, Jojadas sønn, og profeten Natan og Sime'i og Re'i og de helter David hadde, var ikke med Adonja.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 Adonja slaktet får og okser og gjøkalver ved Sohelet-stenen, som er ved En-Rogel, og han innbød alle sine brødre, kongens sønner, og alle Judas menn som var i kongens tjeneste.
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Men profeten Natan og Benaja og heltene og sin bror Salomo innbød han ikke.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Da sa Natan til Batseba, Salomos mor: Du har vel hørt at Adonja, Haggits sønn, er blitt konge, og vår herre David vet ikke noget om det?
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 La mig nu få gi dig et råd, så du kan redde både ditt eget og din sønn Salomos liv!
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Gå inn til kong David og si til ham: Har du ikke, herre konge, med ed lovt din tjenerinne: Salomo, din sønn, skal være konge efter mig; han skal sitte på min trone? Hvorledes er det da gått til at Adonja er blitt konge?
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Og mens du ennu er der inne og taler med kongen, skal jeg og komme inn og stadfeste dine ord.
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 Da gikk Batseba inn til kongen i kammeret. Kongen var nu meget gammel, og Abisag fra Sunem tjente ham.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Og Batseba bøide sig og kastet sig ned for kongen, og kongen sa: Hvad vil du?
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 Hun svarte: Min herre! Du har tilsvoret din tjenerinne ved Herren din Gud: Salomo, din sønn, skal bli konge efter mig; han skal sitte på min trone.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 Men se, nu er Adonja blitt konge, og du, herre konge, vet ikke noget om det.
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 Han har slaktet okser og gjøkalver og får i mengdevis og innbudt alle kongens sønner og presten Abjatar og hærføreren Joab; men Salomo, din tjener, har han ikke innbudt.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Og nu, herre konge, er hele Israels øine vendt mot dig, forat du skal la dem vite hvem som skal sitte på min herre kongens trone efter ham.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 Ellers kan det gå så at når min herre kongen ligger hos sine fedre, kommer jeg og min sønn Salomo til å holdes for forbrytere.
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 Mens hun ennu talte med kongen, kom profeten Natan.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 Da blev det meldt kongen: Profeten Natan er her. Og han kom inn og trådte frem for kongen og kastet sig på sitt ansikt til jorden for ham.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Og Natan sa: Herre konge! Du har vel sagt: Adonja skal være konge efter mig, og han skal sitte på min trone?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 For han har idag draget ned og har slaktet okser og gjøkalver og får i mengdevis og innbudt alle kongens sønner og hærførerne og presten Abjatar, og nu eter og drikker de med ham og roper: Leve kong Adonja!
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 Men mig, din tjener, og presten Sadok og Benaja, Jojadas sønn, og Salomo, din tjener, har han ikke innbudt.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Skulde dette være gjort på min herre kongens bud uten at du har latt dine tjenere vite hvem som skal sitte på min herre kongens trone efter ham?
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Da tok kong David til orde og sa: Kall Batseba inn til mig! Og hun kom inn og trådte frem for kongen.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Og kongen svor og sa: Så sant Herren lever, han som har utfridd mig fra all trengsel:
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 Som jeg har tilsvoret dig ved Herren, Israels Gud: Salomo, din sønn, skal være konge efter mig, og han skal sitte på min trone i mitt sted, så vil jeg gjøre på denne dag.
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 Da bøide Batseba sig med ansiktet mot jorden og kastet sig ned for kongen og sa: Min herre kong David leve evindelig!
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Og kong David sa: Kall hit til mig presten Sadok og profeten Natan og Benaja, Jojadas sønn! Og de kom inn og trådte frem for kongen.
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 Kongen sa til dem: Ta eders herres tjenere med eder og la min sønn Salomo ride på mitt eget muldyr og før ham ned til Gihon!
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 Der skal presten Sadok og profeten Natan salve ham til konge over Israel, og I skal støte i basunen og rope: Leve kong Salomo!
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Så skal I følge ham hit op, og når han kommer, skal han sette sig på min trone, og han skal være konge i mitt sted; det er ham jeg har utsett til fyrste over Israel og Juda.
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 Da tok Benaja, Jojadas sønn, til orde og sa til kongen: Så være det! Måtte også Herren, min herre kongens Gud, ville det så!
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 Som Herren har vært med min herre kongen, så være han med Salomo og gjøre hans trone ennu større enn min herres, kong Davids trone!
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 Da drog presten Sadok og profeten Natan og Benaja, Jojadas sønn, og livvakten ned, og de lot Salomo ride på kong Davids muldyr og førte ham til Gihon.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 Og presten Sadok hentet oljehornet fra teltet og salvet Salomo; og de støtte i basunen, og alt folket ropte: Leve kong Salomo!
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 Og alt folket drog op efter ham, og de blåste på fløiter og jublet så høit at jorden revnet ved deres rop.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 Dette hørte Adonja og alle de gjester som var hos ham; de var da nettop ferdig med å ete. Og da Joab hørte basunlyden, sa han: Hvorfor er det slik larm og bulder i byen?
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 Mens han ennu talte, kom Jonatan, presten Abjatars sønn; og Adonja sa: Kom hit! Du er en bra mann og kommer visst med gode tidender.
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 Men Jonatan svarte og sa til Adonja: Nei! Vår herre kong David har gjort Salomo til konge.
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 Kongen sendte med ham presten Sadok og profeten Natan og Benaja, Jojadas sønn, og livvakten, og de lot ham ride på kongens muldyr.
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 Og presten Sadok og profeten Natan salvet ham til konge i Gihon, og så drog de op derfra i glede, og hele byen er i et røre. Det er den larm I hørte.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 Og Salomo har også alt satt sig på kongetronen,
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 og kongens tjenere er kommet og har ønsket vår herre kong David til lykke og sagt: Din Gud la Salomos navn bli ennu herligere enn ditt navn og hans trone ennu større enn din trone! Og kongen tilbad på sitt leie.
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 Kongen har også sagt så: Lovet være Herren, Israels Gud, som idag har laget det så at det sitter en på min trone, så jeg har fått se det med egne øine!
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Da blev alle Adonjas gjester forferdet; de stod op og gikk, hver sin vei.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Adonja var redd Salomo; han stod op og gikk avsted og grep fatt i alterets horn.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 Da blev det meldt Salomo: Adonja er redd kong Salomo, og nu har han grepet fatt i alterets horn og sier: Kong Salomo må ennu idag tilsverge mig at han ikke vil la sin tjener dø for sverdet!
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Da sa Salomo: Vil han være en bra mann, skal det ikke falle et hår av hans hode til jorden; men blir det funnet noget ondt hos ham, skal han dø.
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 Så sendte kong Salomo folk avsted, og de førte ham ned fra alteret, og han kom og kastet sig ned for kong Salomo, og Salomo sa til ham: Gå hjem til ditt hus!
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< 1 Kongebok 1 >