< 1 Yohana 3 >

1 Mulole ni pendo lya namna gani lyatupeile Tate, panga tukemelwa bana ba Nnongo, na yelo nga tubile. Kwa mana yee ulimwengu ututangite kwaa mana umtangite kwaa ywembe,
Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye.
2 Apendwa twenga nambeambe ni bana ba Nnongo, na yaridhika kwaa bado jinsi yatubile. Tutangite panga Kristo paabonekana, twalowa fanana naywembe, mana twambweni kati yaabile.
Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili.
3 Na kila yumo ambaye abile na ujasiri wolo kuhusu muda woisa wauelekezwa kwake, hujitakasa mwene kati ywembe yaabile mtakatifu.
Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.
4 Kila undu ywaendelea kupanga sambi kuitekwaniya saliya. Kwa sababu sambi ni kutekwania saliya.
Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo.
5 Mutangite Kristo atidhihirishwa ili kuziondoa sambi kabisa.
Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo.
6 Ntopo hata yumo ywadumu nkati yake na kuendelea kupanga sambi, Ntopo mundu hata yumo ywadumu katika sambi mana itei amweni au kuntanga ywembe.
Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.
7 Bana bapendwa, kana mkubali kupotoshwa na mundu yeyote. Ywapanga haki ni mwene haki, mana yelo Kristo ywembe abile mwenye haki.
Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama.
8 Ywapanga sambi ni ba ibilisi, kwa sababu ibilisi ni mpanga sambi tangu mwanzo. Kwa mana yee Mwana wa Nnongo atidhihirishwa ili aweze kuziharibu ili aweze kuziharibu kazi za ibilisi.
Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi.
9 Yeyote ywabelekilwe na Nnongo apanga kwaa sambi, kwa sababu mbeyu ya Nnongo utama nkati yake. Aweza kwaa kuendelea kupanga sambi kwa sababu abelekilwe na Nnongo.
Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu.
10 Katika lee bana ba Nnongo na bana ba ibilisi abtangitwe Yeyote ywapanga kwaa chakibile cha haki, cha Nnongo kwaa, wala yolo ambaye aweza kwaa kumpenda nongowe.
Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.
11 Mana wolo nga ujumbe muuyowine boka mwanzo, panga tupalikwa kupendana twenga kwa twenga,
Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake.
12 abile kwaa kati kaini ambaye abile wa nchela na atimbulaga nongowe. Na kwa mwanja namani atimbulaga? Kwa mana matendo gake gabile mabou, na yalo ya nongowe yabile ya haki.
Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama.
13 Alongo bango, kana mushangae, mana ulimwengu utabachukiya.
Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu.
14 Tutangite tuyomwile boka mu'kiwo na kuyingya mu'ukoto, kwa mana twaapenda alongo. Yeyote ambaye abile kwaa na upendo utama katika kiwo.
Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa.
15 Mundu yeyote ywamchukia nongowe ni muuaji. Na mutangite kuwa ukoto wa milele utama kwaa nkati ya muuaji. (aiōnios g166)
Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios g166)
16 Katika lee tutangite lipendo, kwa sababu kristo atiutoa ukoto wake kwa ajili yitu. Twenga tupalikwa kuyatoa maisha yitu kwa ajili ya nongo.
Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu.
17 Lakini yeyote ywabile na ilebe, na ambona nongowe mwenye uhitaji, lakini huuzuia moyo wake wa huruma kwa ajili yake; je upendo wa Nnongo utama kinamani nkati yake?
Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu?
18 Bana bango bapenzi, tupende kwaa mikano wala kwa maneno matupu ila katika vitendo na kweli.
Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi.
19 Katika lee tutangite panga twenga tubile katika kweli, na mioyo yitu inathibitika katika ywembe.
Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu,
20 mana itei kati mioyo yitu yatuhukumu, Nnongo ni nkolo kuliko mioyo yitu, na ywembe utanga makowe yote.
nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.
21 Apenzi, mana yitu yatuhukumu, tubile na ujasiri kwa Nnongo.
Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu.
22 Na chochote tukiloba twakipokya boka kwake, kwa sababu twazikamwa amri yake na tugapanga makowe yagampendeza nnongi yake.
Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa.
23 Na yee nga amri yake-ya panga tupalika kuamini katika lina lya mwana wake Yesu Kristo ma kupendana twenga kwa twenga kati yatupatia amri yake.
Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira.
24 Ywaziheshimu amri zake utama nkati yake, na Nnongo utama nkati yake. Na kwa sababu yee tutangite panga utama nkati yitu. Kwa yolo Roho ywatupile.
Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.

< 1 Yohana 3 >