< URuthe 1 >

1 Kwasekusithi ensukwini abahluleli abahlulela ngazo kwaba khona indlala elizweni. Umuntu weBhethelehema-Juda wasehamba ukuyahlala njengowezizwe elizweni lakoMowabi, yena lomkakhe lamadodana akhe amabili.
Mu nthawi imene oweruza ankalamulira Israeli, munali njala mʼdziko, ndipo munthu wina wa ku Betelehemu mʼdziko la Yuda anapita pamodzi ndi mkazi wake ndi ana ake aamuna awiri, kukakhala ku Mowabu kwa nthawi yochepa.
2 Njalo ibizo lalowomuntu lalinguElimeleki, lebizo lomkakhe lalinguNawomi, lebizo lamadodana akhe amabili lalinguMaheloni loKiliyoni, amaEfratha eBhethelehema-Juda. Basebesiza elizweni lakoMowabi, baba khona.
Dzina la munthuyo linali Elimeleki, dzina la mkazi wake linali Naomi, ndipo mayina a ana awo aamuna anali Maaloni ndi Kiliyoni. Iwo anali Aefurati ochokera ku Betelehemu ku Yuda. Ndipo anapita kukakhala ku Mowabu.
3 UElimeleki umkaNawomi wasesifa, wasetshiywa yena lamadodana akhe womabili.
Kenaka Elimeleki, mwamuna wake wa Naomi anamwalira ndipo Naomiyo anatsala ndi ana ake aamuna awiri aja.
4 Asezithathela abafazi amaMowabikazi, ibizo lomunye lalinguOpha, lebizo lomunye lalinguRuthe. Basebehlala khona phose iminyaka elitshumi.
Iwo anakwatira akazi a Chimowabu; wina dzina lake Oripa ndi wina Rute. Atakhala kumeneko pafupifupi zaka khumi,
5 Basebesifa labo bobabili oMaheloni loKiliyoni; owesifazana wasetshiywa ngabantwana bakhe bobabili layindoda yakhe.
Maloni ndi Kiliyoni anamwaliranso kotero kuti Naomi anatsala yekha wopanda ana ake awiri aja ndi mwamuna wake.
6 Wasesukuma yena labomalokazana bakhe wabuyela esuka eselizweni lakoMowabi, ngoba wayesezwile elizweni lakoMowabi ukuthi iNkosi ihambele abantu bayo ngokubanika ukudla.
Naomi ndi apongozi ake awiri aja ananyamuka kubwerera kwawo kuchokera ku Mowabu popeza anali atamva ali ku Mowabuko kuti Yehova anakomera mtima anthu ake ndi kuwapatsa chakudya.
7 Ngakho waphuma endaweni lapho ayekhona labomalokazana bakhe bobabili kanye laye, bahamba endleleni ukubuyela elizweni lakoJuda.
Naomi pamodzi ndi apongozi ake awiri aja anachoka kumene ankakhala ndi kuyamba ulendo obwerera kwawo ku Yuda.
8 UNawomi wasesithi kubomalokazana bakhe bobabili: Hambani libuyele ngulowo lalowo endlini kanina; iNkosi kayilenzele umusa njengoba lenza kwabafileyo lakimi.
Kenaka Naomi anati kwa apongozi ake awiri aja, “Bwererani, aliyense kwa amayi ake. Yehova akukomereni mtima, monga munachita ndi malemu aja ndi ine ndemwe.
9 INkosi kayilinike ukuthi lithole ukuphumula, ngulowo lalowo endlini yomkakhe. Wasebanga, basebephakamisa ilizwi labo bakhala inyembezi.
“Yehova akuthandizeni kuti aliyense wa inu apeze pokhala pabwino komanso mwamuna.” Kenaka anawapsompsona koma awiriwo analira mokweza.
10 Basebesithi kuye: Isibili, sizabuyela lawe ebantwini bakini.
Ndipo anati kwa Naomi, “Ife tipita nawo kwa anthu akwanu.”
11 Kodwa uNawomi wathi: Buyelani, madodakazi ami, lizahambelani lami? Kambe ngiselamadodana esiswini sami ukuthi abe ngomkenu?
Koma Naomi anati, “Bwererani kwanu ana anga. Chifukwa chiyani mukufuna kupita ndi ine? Kodi ine ndingaberekenso ana ena kuti akhale amuna anu?
12 Buyelani, madodakazi ami, zihambeleni, ngoba sengimdala kakhulu ukuthi ngibe lendoda. Loba ngingathi ngilethemba lokuthi lami ngalobubusuku ngibe lendoda, njalo ngizale amadodana,
Bwererani kwanu ana anga muzipita kwanu. Ine ndakalamba kwambiri kotero kuti sindingakwatiwenso. Ngakhale ndikananena kuti ndili nacho chikhulupiriro, ngakhale ndikanakhala ndi mwamuna usiku uno, ndipo nʼkubala ana aamuna,
13 belingawalindela yini aze akhule? Belingazivimbela lingabi lendoda yini? Hatshi, madodakazi ami, ngoba kuyababa kakhulu kimi kulakini ukuthi isandla seNkosi siphume ukumelana lami.
kodi inu mukanadikira kuti akule? Kodi mukanakhalabe osakwatiwa kudikira iwowo? Ayi ana anga. Zimenezi zikundiwawa kwambiri kuposa inu, chifukwa ndi ineyo amene Yehova wafuna kuti ndizunzike.”
14 Basebephakamisa ilizwi labo bakhala inyembezi futhi. UOpha wasemanga uninazala, kodwa uRuthe wanamathela kuye.
Atamva zimenezi analiranso kwambiri, ndipo Oripa anapsompsona apongozi ake nawatsanzika, koma Rute anakakamirabe.
15 Wasesithi: Khangela, umkamfowenu usebuyele ebantwini bakibo lakubonkulunkulu bakhe; buyela umlandele umkamfowenu.
Naomi anati “Taona, mʼbale wako wabwerera kwawo kwa anthu ake ndi kwa milungu yake. Bwerera nawenso umulondole mʼbale wako.”
16 Kodwa uRuthe wathi: Ungangincengi ukuthi ngikutshiye, ngibuyele ngiyekele ukukulandela; ngoba lapho oya khona, ngizakuya khona, lalapho olala khona, ngizalala khona. Abantu bakho bangabantu bami, loNkulunkulu wakho unguNkulunkulu wami;
Koma Rute anayankha kuti, “Musandikakamize kuti ndikusiyeni kapena kuti ndibwerere osakutsatani. Kumene inu mupite ine ndipita komweko, ndipo kumene mukakhale inenso ndikakhala komweko. Abale anu adzakhala abale anga ndipo Mulungu wanu adzakhala Mulungu wanga.
17 lapho ozafela khona, ngizafela khona, ngingcwatshelwe lapho. INkosi kayenze njalo kimi ngokunjalo yengezelele, ngoba yikufa kuphela okuzakwehlukanisa phakathi kwami lawe.
Kumene mukafere inenso ndidzafera komweko ndipo komweko ndikayikidwa mʼmanda. Yehova andichite choyipa chingakule motani, ngati china chingatirekanitse ife kupatula imfa.”
18 Kwathi esebonile ukuthi uzimisele ukuhamba laye waseyekela ukukhuluma kuye.
Naomi atazindikira kuti Rute watsimikiza kupita naye, analeka kumukakamiza.
19 Basebehamba bobabili baze bafika eBhethelehema. Kwasekusithi sebefikile eBhethelehema umuzi wonke wayaluzela ngenxa yabo, bathi: Lo nguNawomi yini?
Choncho amayi awiriwo anapitiriza ulendo wawo mpaka anakafika ku Betelehemu. Pamene ankafika mu Betelehemu, anthu onse a mʼmudzimo anatekeseka chifukwa cha iwowo ndipo amayi ambiri ankanena kuti, “Kodi uyu nʼkukhala Naomi?”
20 Wasesithi kibo: Lingangibizi ngokuthi Nawomi, lingibize ngokuthi Mara; ngoba uSomandla ungiphethe ngokubaba okukhulu.
Iye anawawuza kuti, “Musanditchenso Naomi. Muzinditchula ine kuti Mara, chifukwa Wamphamvuzonse wandizunza kwambiri.
21 Mina ngasuka ngigcwele, njalo iNkosi ingibuyise ngingelalutho. Lingibizelani ngokuthi Nawomi lokhu iNkosi ifakaze imelane lami, loSomandla ungihluphile?
Ine ndinapita wolemera, koma Yehova wabwera nane wopanda kanthu. Nanga munditchulirenji Naomi pamene Yehova wandisautsa. Wamphamvuzonse uja wandigwetsera mavuto owawa.”
22 Wabuyela ngokunjalo uNawomi loRuthe umMowabikazi umalokazana wakhe kanye laye, owabuyela evela elizweni lakoMowabi. Bona-ke bafika eBhethelehema ekuqaliseni kwesivuno sebhali.
Naomi anabwerera kuchoka ku dziko la Mowabu pamodzi ndi Rute mpongozi wake. Ndipo anafika ku Betelehemu nthawi yoyamba kukolola barele.

< URuthe 1 >