< URuthe 4 >

1 UBhowazi wasesenyukela esangweni, wahlala phansi lapho. Khangela-ke, kwedlula isihlobo esingumhlengi leso uBhowazi ayekhulume ngaso. Wasesithi: Phambuka uhlale phansi lapha, we zibanibani. Wasephambuka, wahlala phansi.
Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.
2 Wasethatha amadoda alitshumi ebadaleni bomuzi, wathi: Hlalani phansi lapha. Asehlala phansi.
Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.
3 Wasesithi kulesosihlobo esingumhlengi: Isiqinti sensimu esasingesomfowethu uElimeleki, uyasithengisa uNawomi, osebuyile evela elizweni lakoMowabi.
Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja.
4 Ngakho mina ngithe: Ngikwembule endlebeni yakho ngisithi: Sithenge phambi kwabahlali laphambi kwabadala babantu bakithi. Uba uzasihlenga, sihlenge. Kodwa uba engekho ongasihlenga, ungitshele, ukuze ngazi; ngoba engekho ngaphandle kwakho ongasihlenga, mina-ke ngilandela wena. Wasesithi: Mina ngizasihlenga.
Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”
5 UBhowazi wasesithi: Mhla uthenga insimu esandleni sikaNawomi, uzayithenga lakuRuthe umMowabikazi, umfazi womuyi, ukuze umise ibizo lomuyi elifeni lakhe.
Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”
6 Lesosihlobo esingumhlengi sasesisithi: Ngingeke ngazihlengela sona, hlezi ngone ilifa lami. Zihlengele wena ilungelo lami lokuhlenga, ngoba kangilamandla okuhlenga.
Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”
7 Lokhu-ke kwakukhona mandulo koIsrayeli mayelana lokuhlenga lokuntshintsha, ukuqinisa lonke udaba: umuntu akhiphe inyathela lakhe, alinike umakhelwane wakhe; lokhu-ke kwakuyibufakazi koIsrayeli.
(Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).
8 Ngakho isihlobo esingumhlengi sathi kuBhowazi: Zithengele yona; sasesikhipha inyathela laso.
Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.
9 UBhowazi wasesithi kubadala lakubo bonke abantu: Lingabafakazi lamuhla bokuthi ngithengile konke okwakungokukaElimeleki lakho konke okwakungokukaKiliyoni lokukaMaheloni esandleni sikaNawomi.
Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni.
10 LoRuthe laye umMowabikazi, umkaMaheloni, ngizithengele ukuze abe ngumkami, ukuze ngimise ibizo likamuyi elifeni lakhe, ukuze ibizo lomuyi lingaqunywa lisuke phakathi kwabafowabo lesangweni lendawo yakhe. Lingabafakazi lamuhla.
Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”
11 Bonke abantu ababesesangweni labadala basebesithi: Singabafakazi; kungathi iNkosi ingamenza lo owesifazana ongena endlini yakho abe njengoRasheli lanjengoLeya abakha bobabili indlu kaIsrayeli. Njalo wenze ngamandla eEfratha, uzenzele ibizo eBhethelehema,
Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu.
12 lendlu yakho ibe njengendlu kaPerezi uTamari amzalela uJuda, ngenzalo iNkosi ezakunika yona ngalo owesifazana omutsha.
Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”
13 Ngakho uBhowazi wamthatha uRuthe, waba ngumkakhe; wasengena kuye, iNkosi yamnika ukuthi athathe isisu, wazala indodana.
Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.
14 Abesifazana basebesithi kuNawomi: Kayibusiswe iNkosi engakutshiyanga ungelaso isihlobo esingumhlengi lamuhla, ukuthi ibizo laso limenyezelwe koIsrayeli!
Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli.
15 Uzakuba kuwe ngumbuyisi wempilo lomondli wobudala bakho, ngoba umzele umalokazana wakho okuthandayo, ongcono kuwe kulamadodana ayisikhombisa.
Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”
16 UNawomi wasemthatha umntwana, wamfaka esifubeni sakhe, waba ngumlizane wakhe.
Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.
17 Omakhelwanekazi basebemutha ibizo besithi: Kulendodana ezalelwe uNawomi. Babiza ibizo layo uObedi; nguyise kaJese, uyise kaDavida.
Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.
18 Lalezi yizizukulwana zikaPerezi. UPerezi wazala uHezironi,
Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi: Perezi anali abambo a Hezironi.
19 uHezironi wasezala uRamu, uRamu wasezala uAminadaba,
Hezironi anali abambo a Ramu, Ramu anali abambo a Aminadabu,
20 uAminadaba wasezala uNashoni, uNashoni wasezala uSalimoni,
Aminadabu abambo a Naasoni, Naasoni anali abambo a Salimoni,
21 uSalimoni wasezala uBhowazi, uBhowazi wasezala uObedi,
Salimoni abambo a Bowazi, Bowazi abambo a Obedi.
22 uObedi wasezala uJese, uJese wasezala uDavida.
Obedi anali abambo a Yese, ndipo Yese anali abambo a Davide.

< URuthe 4 >