< Amahubo 97 >

1 INkosi iyabusa; kawuthokoze umhlaba, kazijabule izihlenge ezinengi.
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Amayezi lomnyama kuyiphahlile; ukulunga lesahlulelo kuyisisekelo sesihlalo sayo sobukhosi.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Umlilo uhamba phambi kwayo, utshisa izitha zayo inhlangothi zonke.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Imibane yayo ikhanyisa umhlaba; umhlaba wabona, wathuthumela.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Izintaba zancibilika njengengcino phambi kweNkosi, phambi kweNkosi yomhlaba wonke.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Amazulu atshumayela ukulunga kwayo, labantu bonke babona inkazimulo yayo.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Bayayangeka bonke abakhonza izithombe, abazikhukhumeza ngezithixo; ikhonzeni, lonke bonkulunkulu.
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 IZiyoni yezwa, yathokoza, lamadodakazi akoJuda athaba ngenxa yezahlulelo zakho, Nkosi.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Ngoba wena, Nkosi, uphakeme phezu komhlaba wonke, uphakanyiswe kakhulu phezu kwabonkulunkulu bonke.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Lina elithanda iNkosi, zondani okubi; iyagcina imiphefumulo yabangcwele bayo, ibakhulule esandleni sababi.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Ukukhanya kuhlanyelelwe olungileyo, lentokozo abaqotho ngenhliziyo.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Thokozani eNkosini, lina balungileyo, libonge ekukhumbuleni ubungcwele bayo.
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.

< Amahubo 97 >