< Amahubo 87 >
1 Isisekelo sayo siphezu kwentaba ezingcwele.
Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 INkosi iyawathanda amasango eZiyoni kulazo zonke indawo zokuhlala zikaJakobe.
Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 Izinto ezidumileyo zikhulunywa ngawe, muzi kaNkulunkulu! (Sela)
Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
4 Ngizaqamba iRahabi leBhabhiloni kwabangaziyo; khangela, iFilisti leTire kanye leEthiyophiya; lo wazalelwa khona.
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
5 LangeZiyoni kuzakuthiwa: Lo lalowayana bazalelwa kuyo. LoPhezukonke uqobo uzayiqinisa.
Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 INkosi izabala ekubhaleni kwayo abantu, ukuthi lo wazalelwa khona. (Sela)
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
7 Labahlabeleli kanye labagidi, yonke imithombo yami ikuwe.
Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”