< Amahubo 78 >
1 Lalelani, bantu bami, umthetho wami, libeke indlebe yenu emazwini omlomo wami.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Ngizavula umlomo wami ngomfanekiso, ngikhuphe izimfihlakalo zendulo,
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 esizizwileyo lesizaziyo, obaba abasitshela zona.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 Kasiyikuzifihlela abantwana babo, kusizukulwana esilandelayo, silandisa izindumiso zeNkosi, lamandla ayo, lezimangaliso ezenzileyo.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Ngoba wamisa ubufakazi koJakobe, wabeka umlayo koIsrayeli, awulaya obaba, ukuze bawazise abantwana babo,
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 ukuze isizukulwana esilandelayo sazi, abantwana abazazalwa, basukume batshele abantwana babo,
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 ukuze babeke ithemba labo kuNkulunkulu, bangayikhohlwa imisebenzi kaNkulunkulu, kodwa bagcine imithetho yakhe;
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 njalo bangabi njengaboyise, isizukulwana esilenkani lesivukelayo, isizukulwana esingaqondisanga inhliziyo yaso, lesimoya waso ungathembekanga kuNkulunkulu.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Abantwana bakoEfrayimi, behlomile betshoka ngamadandili, babuyela emuva mhla wempi.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 Kabasilondolozanga isivumelwano sikaNkulunkulu, bala ukuhamba emlayweni wakhe.
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 Bakhohlwa izenzo zakhe lezimangaliso zakhe ayebatshengisa zona.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Phambi kwaboyise wenza isimangaliso elizweni leGibhithe, egangeni leZowani.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Waqhekeza ulwandle, wabachaphisa, wenza amanzi ema njengenqumbi.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Wabakhokhela ngeyezi emini, lebusuku bonke ngokukhanya komlilo.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Waqhekeza amadwala enkangala, wabanathisa kungathi kuvela ezinzikini ezinkulu.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Waseveza izifula edwaleni, wenza amanzi ehla njengemifula.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Kodwa baphinda futhi ukona kuye, ngokumvukela oPhezukonke enkangala.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Bamlinga uNkulunkulu enhliziyweni yabo ngokucela ukudla kwenkanuko yabo.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Basebekhuluma bemelene loNkulunkulu bathi: UNkulunkulu angalungisa itafula enkangala yini?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Khangela, watshaya idwala, kwampompoza amanzi, lezifula zagabha; anganika lesinkwa yini? angalungisela abantu bakhe inyama na?
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Ngakho iNkosi yezwa yathukuthela; umlilo wasubaselwa uJakobe, njalo lolaka lwavukela uIsrayeli,
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 ngoba kabakholwanga kuNkulunkulu, kabathembanga esindisweni lwakhe.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Lanxa walaya amayezi ngaphezulu, wavula iminyango yamazulu,
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 wabanisela imana ukuthi badle, wabapha amabele amazulu.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Umuntu wadla isinkwa sabalamandla; wabathumela ukudla ukuze basuthe.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Wenza umoya wempumalanga wavunguza emazulwini; langamandla akhe waqhuba umoya weningizimu.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 Wasenisela phezu kwabo inyama njengothuli, lenyoni ezilempiko njengetshebetshebe lolwandle;
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 wazenza zawela phakathi kwenkamba yabo, zagombolozela indawo zabo zokuhlala.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 Ngakho badla basutha kakhulu, ngoba wabalethela isiloyiso sabo.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 Kabehlukananga lenkanuko yabo; ukudla kusesemlonyeni wabo,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 ulaka lukaNkulunkulu lwaselubavukela, wabulala kwabakhulupheleyo babo, watshaya abakhethiweyo bakoIsrayeli.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 Kulokhu konke bajinga besona, njalo kabakholwanga ngenxa yezimangaliso zakhe.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Ngakho waziqeda izinsuku zabo ngeze, leminyaka yabo ovalweni.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Lapho ebabulala, bamdinga, baphenduka, bamdingisisa uNkulunkulu.
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 Bakhumbula ukuthi uNkulunkulu ulidwala labo, loNkulunkulu oPhezukonke ungumhlengi wabo.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 Kodwa bamyenga ngomlomo wabo, baqamba amanga kuye ngolimi lwabo.
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 Ngoba inhliziyo yabo yayingaqondanga kuye, njalo bengathembekanga esivumelwaneni sakhe.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Kodwa yena elesihawu wathethelela ububi babo, kababhubhisanga; yebo, kanengi walunqanda ulaka lwakhe, kakuvusanga konke ukuthukuthela kwakhe.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 Ngoba wakhumbula ukuthi bayinyama, umoya odlulayo, ongabuyiyo.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Kanengi kangakanani bemvukela ehlane, bemdabukisa enkangala.
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Yebo baphenduka bamlinga uNkulunkulu, bamdabukisa oNgcwele kaIsrayeli.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 Kabasikhumbulanga isandla sakhe, usuku abahlenga ngalo esitheni.
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 Ukuthi wamisa njani izibonakaliso zakhe eGibhithe, lezimangaliso zakhe emmangweni weZowani,
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 lokuthi waphendula imifula yabo yaba ligazi, lezifula zabo, ukuze banganathi.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Wathumela phakathi kwabo umtshitshi wezibawu, ezabadlayo, lamaxoxo ababhubhisayo.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 Wasenika imihogoyi isivuno sabo, lomsebenzi wabo isikhonyane.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Wabulala ivini labo ngesiqhotho, lemikhiwa yabo yesikhamore ngongqwaqwane.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 Wasenikela izifuyo zabo esiqhothweni, lemihlambi yabo kuyo imibane.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Waphosela phezu kwabo ukuvutha kolaka lwakhe, ukuthukuthela, lokucunuka, lokuhlupheka, ngokuthuma izithunywa zobubi.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Walungisela ulaka lwakhe indlela, kanqandanga umphefumulo wabo ekufeni, kodwa wanikela impilo yabo kumatshayabhuqe wesifo.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 Wasetshaya wonke amazibulo eGibhithe, okokuqala kwamandla emathenteni kaHamu.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Wasebakhupha abantu bakhe njengezimvu, wabakhokhela enkangala njengomhlambi.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 Wasebakhokhela bephephile ukuze bangesabi; kodwa ulwandle lwasibekela izitha zabo.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 Wasebafikisa emkhawulweni wendawo yakhe engcwele, le intaba, isandla sakhe sokunene esayizuzayo.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 Wasebaxotsha abezizwe phambi kwabo; wababela ilifa ngomzila, wahlalisa izizwe zakoIsrayeli emathenteni azo.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Kanti bamlinga, bamvukela uNkulunkulu oPhezukonke, kabazigcinanga izifakazelo zakhe.
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Kodwa babuyela emuva, benza ngokungathembeki njengaboyise, baphanjulwa njengedandili elikhohlisayo.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Ngoba bamthukuthelisa ngezindawo zabo eziphakemeyo, bavusa umona wakhe ngezithombe zabo ezibaziweyo.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 UNkulunkulu esizwa wathukuthela, wamenyanya kakhulu uIsrayeli.
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Ngakho walitshiya ithabhanekele leShilo, ithente alimisa phakathi kwabantu.
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 Wasenikela amandla akhe ekuthunjweni, lenkazimulo yakhe esandleni sesitha.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Wasenikela abantu bakhe enkembeni, waselithukuthelela ilifa lakhe.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Umlilo waqeda amajaha abo, lezintombi zabo kazihlatshelelwanga.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Abapristi babo bawa ngenkemba, labafelokazi babo kabalilanga.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Khona iNkosi yavuka njengobelele, njengeqhawe eliklabalala ngenxa yewayini.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 Yazitshaya izitha zayo emuva, yazithela ihlazo phakade.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Yasilahla ithente likaJosefa, kayikhethanga isizwe sakoEfrayimi.
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Kodwa yakhetha isizwe sakoJuda, intaba yeZiyoni eyithandayo.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 Yayakha indlu yayo engcwele njengezingqonga, njengomhlaba ewusekeleyo kuze kube nininini.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 Yasikhetha uDavida inceku yayo, yamthatha ezibayeni zezimvu;
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 ekulandeleni izimvukazi ezenyisayo, yamletha ukwelusa uJakobe abantu bayo, loIsrayeli ilifa layo.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 Njalo wabelusa njengobuqotho benhliziyo yakhe, wabakhokhela ngobugabazi bezandla zakhe.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.