< Amahubo 58 >
1 Isibili likhuluma okulungileyo yini, babusi? Lehlulela ngokuqonda yini, madodana abantu?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Yebo, enhliziyweni lenza okubi, lilinganisa udlakela lwezandla zenu emhlabeni.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Ababi baba ngabemzini kusukela esiswini, bayaduha kusukela esizalweni, beqamba amanga.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Ubuhlungu babo bunjengobuhlungu benyoka, banjengebululu elingezwayo, elivimba indlebe yalo,
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 ukuze lingezwa ilizwi labalumbi abalumba amalumbo ngokuhlakanipha.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Nkulunkulu, yephula amazinyo abo emlonyeni wabo, uphohloze amazinyo emihlathi yamabhongo ezilwane, Nkosi.
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Kabancibilike njengamanzi agelezayo; nxa egobisa idandili lakhe ukutshoka umtshoko wakhe, babe njengabaqunywe iziqa.
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Kahambe njengomnenke oncibilikayo; njengomphunzo owesifazana, kabangaliboni ilanga.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Imbiza zenu zingakaluzwa ukhuni lwameva, uzabaphephula esiphephweni njengabaphilayo njengentukuthelweni.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Olungileyo uzathokoza lapho ebona impindiselo, uzageza inyawo zakhe egazini lomubi.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Ukuze umuntu athi: Impela ukhona umvuzo wolungileyo; impela ukhona uNkulunkulu owahlulela emhlabeni.
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”