< Amahubo 3 >
1 Nkosi, zande kangakanani izitha zami! Banengi abangivukelayo.
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 Banengi abathi ngomphefumulo wami: Kakulasindiso lwakhe kuNkulunkulu. (Sela)
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 Kodwa wena Nkosi, uyisihlangu sami, udumo lwami, lomphakamisi wekhanda lami.
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 Ngakhala ngelizwi lami eNkosini, yasingiphendula isentabeni yayo engcwele. (Sela)
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 Mina ngalala phansi, ngajumeka; ngavuka, ngoba iNkosi yangisekela.
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 Kangiyikwesaba izinkulungwane ezilitshumi zabantu abangihanqileyo bemelana lami.
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 Vuka, Nkosi! Ngisindisa, Nkulunkulu wami. Ngoba zonke izitha zami uzitshayile emhlathini, wephule amazinyo ababi.
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 Usindiso ngolweNkosi. Isibusiso sakho siphezu kwabantu bakho. (Sela)
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)