< Amahubo 2 >
1 Kungani izizwe zixokozela, labantu benakana okuyize?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Amakhosi omhlaba azimisela, lababusi benza ugobe ndawonye bemelene leNkosi njalo bemelene logcotshiweyo wayo, besithi:
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Asiqamule izibopho zabo, silahle intambo zabo zisuke kithi.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 Ohlezi emazulwini uzahleka, iNkosi izabahleka usulu.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Khona izakhuluma kubo entukuthelweni yayo, ibethuse ngokuvutha kolaka lwayo.
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 Kube kanti mina ngibekile iNkosi yami phezu kweZiyoni, intaba yami engcwele.
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 Ngizalandisa ngesimiso: INkosi ithe kimi: Wena uyiNdodana yami, lamuhla ngikuzele.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Cela kimi, ngizanika izizwe zibe yilifa lakho, lemikhawulo yomhlaba ibe yimfuyo yakho.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Uzazephula ngentonga yensimbi, uziphahlaze njengembiza yebumba.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Ngakho-ke hlakaniphani makhosi, lilayeke bahluleli bomhlaba.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Ikhonzeni iNkosi ngokwesaba, lithokoze ngokuthuthumela,
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 liyange iNdodana, hlezi ithukuthele, libhubhe endleleni, nxa ulaka lwayo seluvutha kancinyane. Babusisiwe bonke abaphephela kuyo.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.