< Amahubo 137 >

1 Emifuleni yeBhabhiloni sahlala phansi khona, yebo sakhala inyembezi, lapho sikhumbula iZiyoni.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 Amachacho ethu sawaphanyeka eminyezaneni phakathi kwayo.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 Ngoba khonapho abasithumbayo basicela amazwi engoma, labasimotshayo bacela injabulo besithi: Sihlabeleleni enye yezingoma zeZiyoni.
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Singahlabela njani ingoma yeNkosi elizweni lemzini?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Uba ngikukhohlwa, Jerusalema, isandla sami sokunene kasikhohlwe ubungcitshi.
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Ulimi lwami kalunamathele elwangeni lwami, uba ngingakukhumbuli, uba ngingaphakamisi iJerusalema phezu kwentokozo yami enkulu.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Khumbula, Nkosi, ngabantwana bakoEdoma, ngosuku lweJerusalema, abathi: Dilizani, dilizani, kuze kube sesisekelweni sayo.
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 Ndodakazi yeBhabhiloni, ozabhujiswa, ubusisiwe ozaphindisela kuwe isenzo osenze kithi.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Ubusisiwe ozabamba asakaze abantwana bakho edwaleni.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Amahubo 137 >