< Amahubo 135 >
1 Dumisani iNkosi! Dumisani ibizo leNkosi, dumisani lina zinceku zeNkosi,
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 elimi endlini yeNkosi, emagumeni endlu kaNkulunkulu wethu.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Dumisani iNkosi, ngoba iNkosi ilungile; hlabelelani indumiso ebizweni layo, ngoba kumnandi.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Ngoba iNkosi izikhethele uJakobe, uIsrayeli abe ngokuligugu kwakhe okukhethekileyo.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Ngoba mina ngiyazi ukuthi iNkosi inkulu, ukuthi iNkosi yethu iphezu kwabo bonke onkulunkulu.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Konke iNkosi ekuthandayo iyakwenza, emazulwini lemhlabeni, ezinlwandle lenzikini zonke.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Yenza izinkungu zenyuke emikhawulweni yomhlaba, yenzela izulu imibane, ikhupha umoya eziphaleni zayo.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 Eyatshaya izibulo leGibhithe, kusukela emuntwini kuze kube senyamazaneni.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Yathumela izibonakaliso lezimangaliso phakathi kwakho, Gibhithe, phezu kukaFaro laphezu kwenceku zakhe zonke.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Eyatshaya izizwe ezinengi, yabulala amakhosi alamandla,
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 uSihoni inkosi yamaAmori, loOgi inkosi yeBashani, layo yonke imibuso yeKhanani,
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 yanikela ilizwe labo laba yilifa, ilifa likaIsrayeli, isizwe sayo.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Nkosi, ibizo lakho limi kuze kube phakade, ukukhunjulwa kwakho, Nkosi, kusizukulwana ngesizukulwana.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Ngoba iNkosi izakwehlulela abantu bayo, izazisola mayelana lezinceku zayo.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Izithombe zezizwe ziyisiliva legolide, umsebenzi wezandla zomuntu.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Zilemilomo, kodwa kazikhulumi; zilamehlo, kodwa kaziboni;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 zilendlebe, kodwa kazizwa; lomoya kawukho emlonyeni wazo.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Abazenzayo bafanana lazo, laye wonke othembela kuzo.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Wena ndlu kaIsrayeli, bongani iNkosi; wena ndlu kaAroni, bongani iNkosi;
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 wena ndlu kaLevi, bongani iNkosi. Lina eliyesabayo iNkosi, bongani iNkosi.
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Kayibongwe iNkosi iseZiyoni, ehlala eJerusalema. Dumisani iNkosi!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.