< Amahubo 121 >
1 Ngizaphakamisela amehlo ami ezintabeni, lapho usizo lwami oluzavela khona.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Usizo lwami luvela eNkosini, eyenza amazulu lomhlaba.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Kayiyikuvuma ukuthi unyawo lwakho lutshelele; umlondolozi wakho kayikuwozela.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Khangela, umlondolozi kaIsrayeli kayikuwozela njalo kayikulala.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 INkosi ingumlondolozi wakho; iNkosi ingumthunzi wakho esandleni sakho sokunene.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 Ilanga kaliyikukutshaya emini, lenyanga ebusuku.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 INkosi izakulondoloza kukho konke okubi; izalondoloza umphefumulo wakho.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 INkosi izalondoloza ukuphuma kwakho lokungena kwakho, kusukela khathesi kuze kube phakade.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.