< Amahubo 12 >

1 Siza, Nkosi, ngoba owesaba uNkulunkulu kasekho, ngoba abathembekileyo banyamalele basuka ebantwaneni babantu.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
2 Bakhuluma okuyize, ngulowo lalowo lomakhelwane wakhe; indebe ezilalisayo, bakhuluma nganhliziyombili.
Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
3 INkosi izaquma zonke indebe ezilalisayo, ulimi olukhuluma izinto zokuzidla;
Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
4 abathi: Sizanqoba ngolimi lwethu, indebe zethu ngezethu; ngubani oyinkosi phezu kwethu?
Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
5 Ngenxa yokubandezelwa kwabayanga, ngenxa yokububula kwabaswelayo, sengizavuka, kutsho iNkosi. Ngizabeka ekulondolozekeni amvuthelayo.
“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
6 Amazwi eNkosi angamazwi ahlambulukileyo, isiliva esizanywe esithandweni senhlabathi, sihlanjululwe kasikhombisa.
Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
7 Wena, Nkosi, uzabagcina, ubavikele kulesisizukulwana kuze kube nininini.
Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
8 Ababi bayahambahamba inhlangothi zonke, lapho amanyala ephakanyiswa phakathi kwabantwana babantu.
Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.

< Amahubo 12 >