< Amahubo 115 >

1 Kakungabi kithi, Nkosi, kakungabi kithi, kodwa ebizweni lakho nika udumo, ngenxa yomusa wakho, ngenxa yeqiniso lakho.
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Kungani izizwe zizakuthi: Ungaphi pho uNkulunkulu wabo?
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 Kodwa uNkulunkulu wethu usemazulwini, wenza konke akuthandayo.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Izithombe zabo yisiliva legolide, umsebenzi wezandla zomuntu.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 Zilomlomo, kodwa kazikhulumi; zilamehlo, kodwa kaziboni;
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 zilendlebe, kodwa kazizwa; zilempumulo, kodwa kazinuki;
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 zilezandla, kodwa kaziphathi; inyawo zilazo, kodwa kazihambi; kazikhulumi ngomphimbo wazo.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Abazenzayo kabafanane lazo, wonke othembela kuzo.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Israyeli, themba eNkosini. Ilusizo lwabo lesihlangu sabo.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Ndlu kaAroni, themba eNkosini. Ilusizo lwabo lesihlangu sabo.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Lina elesaba iNkosi, thembani eNkosini. Ilusizo lwabo lesihlangu sabo.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 INkosi isikhumbule, izabusisa, ibusise indlu kaIsrayeli, ibusise indlu kaAroni;
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 izabusisa labo abayesabayo iNkosi, abancinyane kanye labakhulu.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 INkosi izalandisa, lina labantwana benu.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Libusisiwe eNkosini, eyenza amazulu lomhlaba.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Amazulu, amazulu ngaweNkosi, kodwa umhlaba iwunike abantwana babantu.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Abafileyo kabayidumisi iNkosi, hatshi-ke loba ngubani owehlela ekuthuleni.
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 Kodwa thina sizayibonga iNkosi kusukela khathesi kuze kube nininini. Dumisani iNkosi!
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Amahubo 115 >