< Amahubo 114 >

1 Ekuphumeni kukaIsrayeli eGibhithe, indlu kaJakobe ebantwini bolimi lwezizwe,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 uJuda waba yindlu yakhe engcwele, uIsrayeli waba ngumbuso wakhe.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Ulwandle lwakubona lwabaleka, iJordani yabuyela emuva.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Intaba zaqolotsha njengezinqama, amaqaqa njengamawundlu.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Ulani wena lwandle, ukuthi ubaleke? Wena Jordani, ukuthi ubuyele emuva?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Lina zintaba, ukuthi liqolotshe njengezinqama? Lina maqaqa, njengamawundlu?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Thuthumela, mhlaba, phambi kweNkosi, phambi kukaNkulunkulu kaJakobe,
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 owaphendula idwalalibe lichibi lamanzi, ilitshe elilukhuni libe ngumthombo wamanzi.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Amahubo 114 >