< Amahubo 105 >
1 Bongani iNkosi, libize ibizo layo, lazise phakathi kwezizwe izenzo zayo.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Hlabelelani kuyo, lihlabelele amahubo kuyo, likhulume ngezenzo zayo zonke ezimangalisayo.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Zincomeni ebizweni layo elingcwele; kayithokoze inhliziyo yabadinga iNkosi.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Dingani iNkosi lamandla ayo, lidinge ubuso bayo njalonjalo.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Khumbulani izenzo zayo ezimangalisayo eyazenzayo, izimangaliso zayo lezahlulelo zomlomo wayo,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 nzalo kaAbrahama inceku yayo, bantwana bakaJakobe abakhethiweyo bayo.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Yona iyiNkosi uNkulunkulu wethu; izahlulelo zayo zisemhlabeni wonke.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Iyakhumbula isivumelwano sayo kuze kube nininini, ilizwi eyalilaya kuzizukulwana eziyinkulungwane,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 eyasenza loAbrahama, lesifungo sayo kuIsaka;
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 eyasiqinisa kuJakobe saba yisimiso, kuIsrayeli saba yisivumelwano esilaphakade,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 isithi: Ngizakunika wena ilizwe leKhanani, isabelo selifa lakho.
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 Besebalutshwana ngenani, yebo, bebalutshwana, labemzini kulo;
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 basebezula besuka esizweni besiya esizweni, besuka komunye umbuso besiya kwabanye abantu;
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 kayivumelanga muntu ukubahlupha; yasikhuza amakhosi ngenxa yabo,
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 isithi: Lingathinti abagcotshiweyo bami, lingoni abaprofethi bami.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Yasibiza indlala phezu kwelizwe, yephula udondolo lonke lwesinkwa.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Yathuma indoda phambi kwabo: UJosefa wathengiswa waba yisigqili.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Bazwisa ubuhlungu inyawo zakhe ngamaketane, yena ngokwakhe wafika ensimbini.
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 Kwaze kwaba yisikhathi sokufika kwelizwi lakhe, ilizwi likaJehova lamlinga.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Inkosi yathuma yamthukulula, umbusi wabantu wasemkhulula.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Yambeka waba yinkosi yendlu yayo, lombusi wemfuyo yayo yonke,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 ukubopha iziphathamandla zayo ngokuthanda kwakhe, afundise abadala bakhe ukuhlakanipha.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 UIsrayeli wasefika eGibhithe; uJakobe wahlala njengowezizwe elizweni lakoHamu.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Wenza abantu bayo bazale kakhulu, yabenza baba lamandla kulezitha zabo.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Yaphendula inhliziyo yabo ukuzonda abantu bayo, ukuthi baphathe inceku zayo ngobuqili.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Yasithuma uMozisi inceku yayo, uAroni eyayimkhethile.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Babeka phakathi kwabo izinto zezibonakaliso zayo, lezimangaliso elizweni lakoHamu.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Yathumela umnyama, yenza kwaba mnyama; njalo kabavukelanga ilizwi layo.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Yaphendula amanzi abo aba ligazi, yabulala inhlanzi zawo.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Ilizwe labo lanyakazela amaxoxo, emakamelweni amakhosi abo.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Yakhuluma, kwavela umtshitshi wezibawu, intwala emngceleni wabo wonke.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Yabanika isiqhotho saba lizulu, umlilo olamalangabi elizweni labo.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 Yasitshaya isivini sabo lomkhiwa wabo, yephula izihlahla zomngcele wabo.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Yakhuluma, kwasekuvela isikhonyane lemihogoyi, okungelakubalwa,
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 okwaqeda yonke imibhida elizweni labo, kwaqeda isithelo somhlabathi wabo.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Yasitshaya amazibulo wonke elizweni labo, okokuqala kwamandla abo wonke.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Yasibakhupha belesiliva legolide, njalo kwakungekho owakhubekayo phakathi kwezizwe zabo.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 IGibhithe yathokoza ekuphumeni kwabo, ngoba uvalo ngabo lwabehlela.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Yendlala iyezi laba yisisibekelo, lomlilo wokukhanyisa ebusuku.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Bacela, yasiletha izagwaca, yabasuthisa ngesinkwa samazulu.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Yavula idwala, kwampompoza amanzi; ahamba endaweni ezomileyo njengomfula.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Ngoba yakhumbula isithembiso sayo esingcwele, loAbrahama inceku yayo.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Yasikhupha abantu bayo ngentokozo, abakhethiweyo bayo ngenjabulo.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Yasibanika amazwe abezizwe, njalo badla ilifa lomtshikatshika wabantu,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 ukuze bagcine izimiso zayo, balondoloze imilayo yayo. Dumisani iNkosi!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.