< Amahubo 1 >

1 Ubusisiwe umuntu ongahambi ngeseluleko sababi, ongemi endleleni yezoni, ongahlali esihlalweni sabagconayo;
Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2 kodwa intokozo yakhe isemlayweni weNkosi, uzindla ngomlayo wayo emini lebusuku.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3 Njalo uzakuba njengesihlahla esihlanyelwe emifuleni yamanzi, esithela isithelo saso ngesikhathi saso, ohlamvu laso kaliyikubuna; lakho konke akwenzayo kuzaphumelela.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4 Ababi kabanjalo, kodwa banjengamakhoba umoya owaphephulayo.
Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5 Ngakho ababi kabayikuma ekwahlulelweni, lezoni enhlanganweni yabalungileyo.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6 Ngoba iNkosi iyayazi indlela yabalungileyo, kodwa indlela yababi izabhubha.
Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

< Amahubo 1 >