< Izaga 1 >

1 Izaga zikaSolomoni, indodana kaDavida, inkosi yakoIsrayeli;
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 ukwazi inhlakanipho lokulaywa, ukuqedisisa amazwi okuqedisisa,
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 ukwemukela ukulaya kwenhlakanipho, ukulunga, lesahlulelo, lokuqonda;
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 ukunika abangelalwazi inhlakanipho, ijaha ulwazi lengqondo.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Ohlakaniphileyo uzakuzwa, andise ukufunda, loqedisisayo uzazuza izeluleko,
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 ukuqedisisa isaga lomzekeliso, amazwi abahlakaniphileyo, lamalibho abo.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Ukwesaba iNkosi kuyikuqala kolwazi; izithutha ziyadelela inhlakanipho lokulaywa.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Ndodana yami, zwana ukulaya kukayihlo, ungawudeli umlayo kanyoko;
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 ngoba kuzakuba ngumqhele womusa ekhanda lakho, lemigaxo entanyeni yakho.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Ndodana yami, uba izoni zikuhuga, ungavumi.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Uba zisithi: Hamba lathi, siyecathamela igazi, sicatshele ongelacala kungelasizatho;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 sibaginye bephila njengengcwaba, yebo, ngokupheleleyo, njengabehlela egodini. (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Sizathola yonke impahla eligugu, sigcwalise izindlu zethu ngempango.
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Phosela inkatho yakho phakathi kwethu; sonke sibe lesikhwama semali sinye.
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Ndodana yami, ungahambi lazo endleleni; unqande unyawo lwakho emkhondweni wazo.
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Ngoba inyawo zazo zigijimela ebubini, ziphangisa ukuchitha igazi.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Isibili, imbule lendlalelwa ize phambi kwamehlo aloba yiyiphi inyoni.
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 Lalaba bacathamela igazi labo, bacatshele imiphefumulo yabo.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Zinjalo indlela zakhe wonke ozuza inzuzo ngokuphanga; ithatha impilo yabaniniyo.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 UkuHlakanipha kuyamemeza ngaphandle, kukhupha ilizwi lakho emidangeni.
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Kuyamemeza endaweni eqakathekileyo yokuxokozela, ekungeneni kwamasango; emzini kutsho amazwi akho,
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 kusithi: Koze kube nini, lina elingelalwazi, lithanda ukungabi lalwazi, labaklolodayo bezifisela ukukloloda, leziphukuphuku zizonda ulwazi?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Phendukelani ekukhuzeni kwami; khangelani, ngizathululela umoya wami kini, ngilazise amazwi ami.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Ngoba ngibizile, kodwa lala; ngelulile isandla sami, kodwa kakho onanzayo;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 ladelela sonke iseluleko sami, kalivumanga ukukhuza kwami;
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 mina-ke ngizahleka ukuchitheka kwenu, ngiklolode ekufikeni kokwesaba kwenu,
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 ekufikeni kokwesaba kwenu njengesiphepho, lokuchitheka kwenu kufika njengesivunguzane, lapho ubuhlungu losizi kulehlela.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Khona bazangibiza, kodwa kangiyikusabela; bazangidingisisa, kodwa kabayikungithola.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Ngenxa yokuthi babezonda ulwazi, bengakhethanga ukwesaba iNkosi.
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Kabavumanga iseluleko sami, bedelela konke ukukhuza kwami.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Ngakho bazakudla okwesithelo sendlela yabo, basuthiswe ngamacebo abo.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Ngoba ukuhlehla kwabangelalwazi kuzababulala, lokonwaba kweziphukuphuku kuzababhubhisa.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Kodwa ongilalelayo uzahlala evikelekile, onwabe ekwesabeni okubi.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Izaga 1 >