< Izaga 4 >
1 Zwanini, bantwana, umlayo kayihlo, linanzelele ukuze lazi ukuqedisisa.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Ngoba ngilinika imfundiso enhle, lingawutshiyi umlayo wami.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Ngoba bengiyindodana kababa, ngithambile, ngingedwa phambi kukamama.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Wasengifundisa wathi kimi: Inhliziyo yakho kayibambelele emazwini ami; gcina imilayo yami, uphile.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Zuza inhlakanipho, uzuze ukuqedisisa, ungakhohlwa; ungaphambuki emazwini omlomo wami.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Ungakutshiyi, njalo kuzakulondoloza; ukuthande, njalo kuzakulinda.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Okokuqala yinhlakanipho; zuza inhlakanipho; langenzuzo yakho yonke uzuze ukuqedisisa.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Kukhulise, njalo kuzakuphakamisa; kuzakunika udumo nxa ukugona.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Kuzanika ikhanda lakho umqhele womusa; kuzakulethela umqhele wodumo.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Zwana, ndodana yami, wemukele amazwi ami, leminyaka yempilo izakuba minengi kuwe.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ngikufundisile endleleni yenhlakanipho; ngikwenze wanyathela emikhondweni yobuqotho.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Ekuhambeni kwakho inyathelo lakho kaliyikufinyezwa, njalo nxa ugijima kawuyikukhubeka.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Bambelela ekulayweni, ungakuyekeli; kugcine, ngoba kuyimpilo yakho.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Ungangeni emkhondweni wabakhohlakeleyo, ungahambi endleleni yababi.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Iyekele, ungedluli ngayo, phambuka kuyo, wedlule.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Ngoba kabalali uba bengenzanga okubi; lobuthongo babo buyasuswa uba bengakhubekisanga muntu.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Ngoba badla isinkwa senkohlakalo, banathe iwayini lobudlwangudlwangu.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Kodwa indlela yabalungileyo injengokukhanya okukhanyayo, kuqhubeka kukhanya kuze kube semini enkulu.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Indlela yababi injengomnyama; kabazi ukuthi bazakhutshwa yini.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Ndodana yami, lalela amazwi ami, ubeke indlebe yakho ekukhulumeni kwami.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Kakungaphunyuki emehlweni akho; ukugcine phakathi kwenhliziyo yakho.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Ngoba kuyimpilo kwabakutholayo, lempilo enhle yenyama yabo yonke.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Gcina inhliziyo yakho phezu kwakho konke okungagcinwa, ngoba kuvela kikho ukuphuma kwempilo.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Susa kuwe ukuphambana komlomo, lokuphambeka kwendebe kususele khatshana lawe.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Amehlo akho kawakhangele phambili, lenkophe zakho ziqonde phambi kwakho.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Linganisa umkhondo wonyawo lwakho, ukuze zonke indlela zakho ziqine.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Ungaphambukeli ngakwesokunene kumbe ngakwesokhohlo; uphambule unyawo lwakho ebubini.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.