< Izaga 31 >

1 Amazwi kaLemuweli inkosi yeMasa, unina amfundisa wona.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 Ini, ndodana yami! Ini-ke, ndodana yesizalo sami! Ini-ke, ndodana yezithembiso zami!
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Unganiki amandla akho kwabesifazana, kumbe izindlela zakho ekubhubhiseni amakhosi.
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 Kakusikwamakhosi, Lemuweli, kakusikwamakhosi ukunatha iwayini, kumbe okweziphathamandla ukuloyisa okunathwayo okulamandla.
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 Hlezi anathe, akhohlwe isimiso, aguqule isahlulelo sawo wonke amadodana enhlupheko.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Phana okunathwayo okulamandla kobhubhayo, lewayini kwabababayo emphefumulweni.
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 Kanathe, akhohlwe ubuyanga bakhe, angabe esakhumbula usizi lwakhe.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Vulela isimungulu umlomo wakho, udaba lwabo bonke abamiselwe incithakalo.
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Vula umlomo wakho, wahlulele ngokulunga, umele ilungelo lomyanga loswelayo.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Ngubani ongathola umfazi okhuthela okulungileyo? Ngoba intengo yakhe iyedlula kakhulu amatshe amahle.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Inhliziyo yomkakhe ithemba kuye, ukuze angasweli impango.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Umenzela okuhle, hatshi okubi, insuku zonke zempilo yakhe.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Udinga uboya bezimvu lefilakisi, asebenze ngenjabulo yezandla zakhe.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Ufanana lemikhumbi yomthengisi; uletha ukudla kwakhe kuvela khatshana.
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 Uvuka kusesebusuku, anike indlu yakhe ukudla, lesabelo kuzincekukazi zakhe.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Anakane ngensimu ayizuze; ngesithelo sezandla zakhe ahlanyele ivini.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Uyabhinca ukhalo lwakhe ngamandla, aqinise ingalo zakhe.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Uyananzelela ukuthi ukuthengisa kwakhe kuhle; isibane sakhe kasicitshi ebusuku.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Welulela izandla zakhe kuluthi lokuphotha, lezandla zakhe zibambe isigodo esilezintambo.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Welulela umyanga isandla sakhe, elulele izandla zakhe koswelayo.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Kesabi iliqhwa elikhithikileyo ngenxa yabendlu yakhe, ngoba bonke abendlu yakhe bagqokiswe okubomvu.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Uzenzela izembeso; isigqoko sakhe sililembu elicolekileyo leliyibubende.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Umkakhe uyaziwa emasangweni, lapho ehlezi labadala belizwe.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Wenza ilembu elicolekileyo kakhulu, alithengise; anike umthengi ibhanti.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Amandla lodumo kuyisigqoko sakhe; uyahleka mayelana losuku olulandelayo.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Uvula umlomo wakhe ngenhlakanipho; lemfundiso yomusa iselimini lwakhe.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Uqaphela inhambo zomuzi wakhe; kadli isinkwa sobuvila.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Abantwana bakhe bayavuka bathi ubusisiwe, lomkakhe laye uyamdumisa:
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 Manengi amadodakazi enze ngenkuthalo, kodwa wena wenyukile phezu kwawo wonke.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Ubuhle buyinkohliso, lokubukeka kuyize; owesifazana owesaba iNkosi yena uzadunyiswa.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Mnikeni okuvela esithelweni sezandla zakhe, lemisebenzi yakhe kayimdumise emasangweni.
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Izaga 31 >