< Izaga 3 >
1 Ndodana yami, ungakhohlwa umlayo wami, kodwa inhliziyo yakho kayigcine imilayo yami.
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Ngoba yengezelela kuwe ubude bezinsuku leminyaka yempilo lokuthula.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Umusa lothembeko kakungakutshiyi, kubophele entanyeni yakho, ukubhale esibhebheni senhliziyo yakho.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Ngalokho uzathola umusa lokuqedisisa okuhle emehlweni kaNkulunkulu labantu.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Themba eNkosini ngenhliziyo yakho yonke, ungeyami ekuqedisiseni kwakho.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Ivume endleleni zakho zonke, yona-ke izaqondisa imikhondo yakho.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Ungabi ngohlakaniphileyo emehlweni akho; yesabe iNkosi, usuke ebubini.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Kuzakuba yikwelatshwa kwenkaba yakho, lokunathwayo kwamathambo akho.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Hlonipha iNkosi ngemfuyo yakho, langezithelo zakho zokuqala zesivuno sakho sonke.
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Khona iziphala zakho zizagcwaliswa ngenala, lezikhamelo zakho zewayini ziphuphume iwayini elitsha.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Ndodana yami, ungadeleli ukulaya kweNkosi, unganengwa yikukhuza kwayo.
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Ngoba iNkosi iyamlaya emthandayo, yebo, njengoyise indodana athokoza ngayo.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Ubusisiwe umuntu othola inhlakanipho, lomuntu ozuza ukuqedisisa.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Ngoba inzuzo yakho ingcono kulenzuzo yesiliva, lokutholakalayo kwakho kulegolide.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Kuligugu elidlula amatshe aligugu, lakho konke ongakufisa kakulinganiswa lakho.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Ubude bezinsuku busesandleni sakho sokunene, kwesokhohlo sakho inotho lodumo.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Izindlela zakho zizindlela zentokozo, lemikhondo yakho yonke iyikuthula.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Kuyisihlahla sempilo kwabakubambayo, lobambelela kukho ubusisiwe.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Ngenhlakanipho iNkosi yasekela umhlaba; yamisa amazulu ngokuqedisisa.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Ngolwazi lwayo izinziki zaqhekezwa, lamayezi athonta amazolo.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Ndodana yami, kakungasuki emehlweni akho; gcina inhlakanipho eqotho lengqondo.
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 Njalo kuzakuba yimpilo yomphefumulo wakho, lesisa entanyeni yakho.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Khona uzahamba indlela yakho uvikelekile, lonyawo lwakho kaluyikukhubeka.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Nxa ulala phansi, kawuyikwesaba, yebo, uzalala, lobuthongo bakho buzakuba mnandi.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Ungesabi uvalo olujumayo, kumbe ukuchitheka kwababi nxa kufika.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Ngoba iNkosi izakuba sethembeni lakho, igcine unyawo lwakho ukuze lungabanjwa.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Ungagodleli umninikho okuhle nxa kusemandleni esandla sakho ukukwenza.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Ungathi kumakhelwane wakho: Hamba, ubuye, kusasa ngizakunika; nxa ulakho.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Ungacebi okubi ngomakhelwane wakho, ngoba yena uhlala lawe evikelekile.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Ungaphikisani lomuntu kungelasizatho, nxa engakonanga.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Ungahawukeli umuntu olobudlwangudlwangu; ungakhethi leyodwa yezindlela zakhe.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Ngoba ophambeneyo uyisinengiso eNkosini, kodwa imfihlo yayo ikwabaqotho.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Isiqalekiso seNkosi sisendlini yomubi, kodwa iyawubusisa umuzi wabalungileyo.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Isibili, yona iyabeyisa abeyisayo, kodwa inika umusa kwabathobekileyo.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Abahlakaniphileyo bazakudla ilifa lodumo, kodwa abayizithutha, isabelo sabo silihlazo.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.