< Izaga 21 >

1 Inhliziyo yenkosi isesandleni sikaJehova injengezifula zamanzi; uyiphendulela loba ngaphi athanda khona.
Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
2 Yonke indlela yomuntu ilungile emehlweni akhe, kodwa iNkosi ihlola izinhliziyo.
Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
3 Ukwenza ukulunga lesahlulelo kukhethekile eNkosini kulomhlatshelo.
Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
4 Ukuphakama kwamehlo, lokuzigqaja kwenhliziyo, lokulima kwabakhohlakeleyo, kuyisono.
Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
5 Imicabango yokhutheleyo isenzuzweni kuphela, kodwa eyakhe wonke ophangisayo isekusweleni kuphela.
Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
6 Ukwenza inotho ngolimi lwamanga kuyize eliphephukayo elalabo abadinga ukufa.
Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
7 Isihluku sababi sizabahudula, ngoba besala ukwenza okulungileyo.
Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
8 Indlela yomuntu igobile njalo ilecala, kodwa ohlanzekileyo, umsebenzi wakhe uqondile.
Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
9 Kungcono ukuhlala engonsini yophahla kulalowesifazana wezinkani lendlini yokuhlanganyela.
Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
10 Umphefumulo wokhohlakeleyo uloyisa ububi; umakhelwane wakhe kemukeli umusa emehlweni akhe.
Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
11 Nxa isideleli sijeziswa, umuntu ongelalwazi uyahlakanipha; lalapho ohlakaniphileyo elaywa wemukela ulwazi.
Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
12 Olungileyo uyananzelela indlu yokhohlakeleyo; uNkulunkulu uwisela abakhohlakeleyo ebubini.
Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
13 Ogcika indlebe yakhe ekukhaleni komyanga, laye uzakhala angaphendulwa.
Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
14 Isipho sensitha siyadedisa intukuthelo, lesivalamlomo esifubeni ulaka olulamandla.
Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
15 Kuyintokozo kolungileyo ukwenza ukulunga, kodwa kuluvalo kubenzi bobubi.
Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
16 Umuntu oduha endleleni yokuqedisisa uzahlala ebandleni lemimoya efileyo.
Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
17 Othanda injabulo uzakuba ngumyanga; othanda iwayini lamafutha kayikunotha.
Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18 Okhohlakeleyo uyinhlawulelo yolungileyo, lesiphambeki esikhundleni sabaqotho.
Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
19 Kungcono ukuhlala elizweni eliyinkangala kulalowesifazana wezingxabano lolaka.
Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
20 Kukhona imfuyo eloyisekayo lamafutha emzini wohlakaniphileyo, kodwa umuntu oyisithutha uyakuginya.
Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
21 Oxotshana lokulunga lomusa uzathola impilo, ukulunga, lodumo.
Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
22 Ohlakaniphileyo ukhwela emzini wamaqhawe, adilizele phansi amandla ethemba lawo.
Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
23 Ogcina umlomo wakhe lolimi lwakhe, ugcina umphefumulo wakhe ezinkathazweni.
Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
24 Isideleli esizikhukhumezayo esizigqajayo libizo lakhe osebenza ngolaka lokuzikhukhumeza.
Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
25 Isiloyiso sevila sizalibulala, ngoba izandla zalo ziyala ukusebenza.
Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
26 Usuku lonke liloyisa isiloyiso, kodwa olungileyo uzakupha, angagodli.
Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
27 Umhlatshelo wabakhohlakeleyo uyisinengiso; kakhulu kangakanani nxa bewuletha ngecebo elibi.
Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
28 Umfakazi wamanga uzabhubha, kodwa umuntu olalelayo uzakhuluma njalonjalo.
Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
29 Umuntu okhohlakeleyo wenza lukhuni ubuso bakhe, kodwa oqotho yena uyananzelela indlela yakhe.
Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
30 Kakulanhlakanipho, njalo kakulakuqedisisa, njalo kakulaseluleko, okumelana leNkosi.
Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
31 Ibhiza lilungiselwa usuku lwempi, kodwa ukukhululwa ngokweNkosi.
Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

< Izaga 21 >