< Izaga 15 >
1 Impendulo ethambileyo ibuyisela emuva ulaka, kodwa ilizwi elilukhuni livusa intukuthelo.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 Ulimi lwabahlakaniphileyo lwenza ulwazi lube luhle, kodwa umlomo wezithutha uthulula ubuthutha.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 Amehlo eNkosi akuyo yonke indawo, eqaphela ababi labalungileyo.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 Ukusilisa kolimi kuyisihlahla sempilo, kodwa ukuphambeka kulo kuyikwephuka emoyeni.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 Isithutha sidelela ukulaya kukayise, kodwa onanza ukukhuzwa uhlakaniphile.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 Endlini yolungileyo kulenotho enengi, kodwa enzuzweni yomubi kulenkathazo.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Indebe zabahlakaniphileyo ziyahlakaza ulwazi, kodwa inhliziyo yezithutha kayinjalo.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Umhlatshelo wabakhohlakeleyo uyisinengiso eNkosini, kodwa umkhuleko wabaqotho uyintokozo yayo.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 Indlela yokhohlakeleyo iyisinengiso eNkosini, kodwa ithanda ozingela ukulunga.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 Ukujezisa kubi kotshiya indlela; ozonda ukukhuzwa uzakufa.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Isihogo lentshabalalo kuphambi kweNkosi; kakhulu kangakanani inhliziyo zabantwana babantu! (Sheol )
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
12 Isideleli kasithandi osikhuzayo, kasiyi kwabahlakaniphileyo.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Inhliziyo ethokozayo yenza ubuso bujabule, kodwa ngosizi lwenhliziyo umoya uyadabuka.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 Inhliziyo yoqedisisayo idinga ulwazi, kodwa umlomo wezithutha udla ubuthutha.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Zonke insuku zohluphekayo zimbi, kodwa inhliziyo ethokozayo ilidili njalonjalo.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Kungcono okuncinyane kanye lokwesaba iNkosi kulenotho enengi lenkathazo kanye layo.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Kungcono isidlo semibhida lapho okulothando khona kulenkabi enonileyo lenzondo kanye layo.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 Umuntu ololaka udungula ingxabano, kodwa ophuza ukuthukuthela uzathulisa ingxabano.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 Indlela yevila injengothango lwameva, kodwa indlela yabaqotho ibuthelelwe.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 Indodana ehlakaniphileyo ithokozisa uyise, kodwa umuntu oyisithutha weyisa unina.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 Ubuthutha buyintokozo koswela ingqondo, kodwa umuntu oqedisisayo uyaqondisa ukuhamba kwakhe.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Amaqhinga angelaseluleko ayachitheka, kodwa ngabeluleki abanengi ayakuma.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 Umuntu ulentokozo ngempendulo yomlomo wakhe; lelizwi ngesikhathi salo, lihle kangakanani.
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 Indlela yempilo kohlakaniphileyo iya phezulu, ukuze asuke esihogweni phansi. (Sheol )
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
25 INkosi izadiliza indlu yozigqajayo, kodwa izamisa umngcele womfelokazi.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 Imicabango yomubi iyisinengiso eNkosini, kodwa amazwi amnandi ahlambulukile.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 Ophanga inzuzo ukhathaza indlu yakhe, kodwa ozonda izipho uzaphila.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 Inhliziyo yolungileyo inakana ukuphendula, kodwa umlomo wababi uthulula izinto ezimbi.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 INkosi ikhatshana labakhohlakeleyo, kodwa iyezwa umkhuleko wabalungileyo.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 Ukukhanya kwamehlo kuthokozisa inhliziyo, lodaba oluhle lwenza amathambo akhuluphale.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 Indlebe elalela ukukhuzwa kwempilo izahlala phakathi kwabahlakaniphileyo.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 Owala ukulaywa weyisa umphefumulo wakhe, kodwa olalela ukukhuzwa uzuza ukuqedisisa.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 Ukuyesaba iNkosi kuyikufundiswa kwenhlakanipho, lokuthobeka kwandulela udumo.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.