< Izaga 13 >
1 Indodana ehlakaniphileyo ilalela ukulaya kukayise, kodwa isideleli kasilaleli ukukhuzwa.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 Umuntu uzakudla okuhle okuvela esithelweni somlomo, kodwa umphefumulo weziphambuki ubudlwangudlwangu.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 Olondoloza umlomo wakhe ugcina umphefumulo wakhe, kodwa ovula indebe zakhe zibe banzi uzakuba lencithakalo.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 Umphefumulo wevila uyafisa, kodwa kakulalutho; kodwa umphefumulo wokhutheleyo uyakhuluphaliswa.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 Olungileyo uyalizonda ilizwi lamanga; kodwa omubi uzenza abe levumba, uthelela ihlazo.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 Ukulunga kulinda oqotho endleleni, kodwa inkohlakalo ichitha isoni.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 Kukhona ozitshaya onothileyo, kanti kalalutho; ozitshaya ongumyanga, kanti unothile kakhulu.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 Inhlawulo yempilo yomuntu yinotho yakhe, kodwa umyanga kezwa ukukhuzwa.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 Ukukhanya kwabalungileyo kuyathokoza, kodwa isibane sabakhohlakeleyo sizacitshwa.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 Ukuzigqaja kuveza ingxabano kuphela, kodwa inhlakanipho ikwabalulekiweyo.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Inotho etholakala ngokuyize izaphunguka, kodwa obuthelela ngesandla uyayandisa.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 Ithemba eliphuzayo ligulisa inhliziyo, kodwa isifiso esizayo siyisihlahla sempilo.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 Odelela ilizwi yena uzachithwa, kodwa owesaba umlayo yena uzavuzwa.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 Imfundiso yohlakaniphileyo ingumthombo wempilo, ukuthi asuke emijibileni yokufa.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Ukuqedisisa okuhle kunika umusa, kodwa indlela yabaphambukayo ilukhuni.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Wonke ohlakaniphileyo wenza ngolwazi, kodwa isithutha sichaya ubuthutha.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 Isithunywa esikhohlakeleyo siwela ebubini, kodwa isithunywa esithembekileyo siyikusilisa.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Ubuyanga lehlazo ngokwalowo oyekela ukufundiswa, kodwa onanzelela ukukhuzwa uzadunyiswa.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 Isifiso esenziweyo simnandi emphefumulweni, kodwa kuyisinengiso ezithutheni ukuphenduka ebubini.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 Ohamba labahlakaniphileyo uzahlakanipha, kodwa umngane wezithutha uzakuba mubi.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Ububi buzazingela izoni, kodwa abalungileyo bazavuzwa ngokuhle.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 Olungileyo uzabenza abantwana babantwana badle ilifa, kodwa inotho yesoni ibekelwa olungileyo.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 Ukudla okunengi kusengqathweni yabayanga, kodwa kukhona okukhukhulwa ngokungabi lokwahlulela.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 Ogodla uswazi lwakhe uzonda indodana yakhe, kodwa oyithandayo uyayidinga masinyane ngesijeziso.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 Olungileyo uyadla kuze kusuthe umphefumulo wakhe, kodwa isisu sabakhohlakeleyo sizaswela.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.