< U-Obhadiya 1 >

1 Umbono kaObhadiya. Itsho njalo iNkosi uJehova mayelana leEdoma: Sizwile umbiko ovela eNkosini, njalo kuthunywe isithunywa phakathi kwezizwe: Sukumani, kasimvukele empini!
Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
2 Khangela, ngikwenze waba mncinyane phakathi kwezizwe, udelelwe kakhulu.
“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
3 Ukuziqhenya kwenhliziyo yakho kukukhohlisile, wena ohlala ezingoxweni zamadwala, ondawo yakhe yokuhlala iphakeme, othi enhliziyweni yakhe: Ngubani ozangehlisela emhlabathini?
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
4 Loba uphakeme njengokhozi, njalo loba ubeka isidleke sakho phakathi kwezinkanyezi, ngizakwethula khona, itsho iNkosi.
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
5 Uba amasela efika kuwe, loba abaphangi ebusuku (uqunywe kangakanani!) bebengayikuntshontsha baze banele yini? Uba abavuni bezithelo zevini bebengafika kuwe, bebengayikutshiya umkhothozo yini?
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
6 Yeka ukuhlolwa kwezinto zikaEsawu, ukudingisiswa kokuligugu kwakhe okufihliweyo!
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
7 Wonke amadoda esivumelwano sakho akuthumele emngceleni; amadoda okuthula kwakho akukhohlisile, akwehlule, adla isinkwa sakho abeke imbule ngaphansi kwakho; kakukho ukuqedisisa kuye.
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
8 Kakuyikuba njalo yini ngalolosuku, itsho iNkosi, ukuthi ngizachitha abahlakaniphileyo eEdoma lokuqedisisa entabeni kaEsawu.
Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
9 Lamaqhawe akho azatshaywa luvalo, Themani, ukuze ngulowo lalowo aqunywe entabeni kaEsawu ngokubulawa.
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
10 Ngenxa yodlakela lwakho umelene lomfowenu uJakobe inhloni zizakusibekela, uqunywe kuze kube phakade.
Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
11 Ngosuku owema ngalo uqondene labo, ngosuku abezizweni abathumba ngalo amabutho akhe, abezizwe abangena emasangweni akhe, abenza inkatho yokuphosa ngeJerusalema, lawe wawunjengomunye wabo.
Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 Kodwa wawungafanelanga ukukhangela ngosuku lomfowenu ngosuku lwenhlupheko yakhe; njalo wawungafanelanga uthokoze ngabantwana bakoJuda ngosuku lokuchitheka kwabo; njalo wawungafanelanga ukhulume ngokuziqhenya ngosuku lokuhlupheka.
Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
13 Ngabe kawungenanga ngesango labantu bami osukwini lwenhlupheko yabo; ngabe kawukhangelanga, lawe, ebubini babo osukwini lwenhlupheko yabo; njalo ngabe kawelulelanga isandla sakho enothweni yabo osukwini lwenhlupheko yabo.
Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
14 Ngabe kawumanga emehlukanweni endlela ukuquma abaphunyukayo bakhe; njalo ngabe kawunikelanga abasalayo bakhe osukwini losizi.
Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
15 Ngoba usuku lweNkosi lusondele ezizweni zonke. Njengokwenza kwakho kuzakwenziwa kuwe; umvuzo wakho uzabuyela ekhanda lakho.
“Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 Ngoba njengoba linathile entabeni yami engcwele, ngokunjalo zonke izizwe zizanatha njalonjalo, yebo, zizanatha, ziginye, zibe kungathi kazizanga zibe khona.
Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 Kodwa entabeni yeZiyoni kuzakuba khona ukuphunyuka, kube lobungcwele; lendlu kaJakobe izakudla ilifa lamafa ayo.
Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
18 Lendlu kaJakobe izakuba ngumlilo, lendlu kaJosefa ibe lilangabi, lendlu kaEsawu ibe libibi; njalo bazazitshisa bazidle; njalo kakuyikuba khona oseleyo endlini kaEsawu; ngoba iNkosi ikhulumile.
Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
19 Labeningizimu bazakudla ilifa lentaba kaEsawu, lalabo abemagcekeni amaFilisti, yebo bazakudla ilifa lensimu yakoEfrayimi lensimu yeSamariya, loBhenjamini iGileyadi.
Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 Labathunjiweyo bale inqaba yabantwana bakoIsrayeli bazakudla ilifa elalingelamaKhanani, kuze kufike eZarefathi; labathunjiweyo beJerusalema abaseSefaredi bazakudla ilifa lemizi yeningizimu.
Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 Labasindisi bakhwele entabeni yeZiyoni ukwahlulela intaba kaEsawu; lombuso uzakuba ngoweNkosi.
Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

< U-Obhadiya 1 >