< Amanani 25 >
1 UIsrayeli wasehlala eShithimi. Abantu basebeqala ukuphinga lamadodakazi akoMowabi.
Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu,
2 Asebabizela abantu emihlatshelweni yabonkulunkulu bawo, labantu badla, bakhothamela onkulunkulu bawo.
amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo.
3 UIsrayeli wasezihlanganisa loBhali-Peyori; lolaka lweNkosi lwamvuthela uIsrayeli.
Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.
4 INkosi yasisithi kuMozisi: Thatha zonke inhloko zabantu, uziphanyeke phambi kweNkosi maqondana lelanga, ukuze ulaka lweNkosi oluvuthayo lubuye lusuke koIsrayeli.
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”
5 UMozisi wasesithi kubahluleli bakoIsrayeli: Bulalani, kube ngulowo lalowo amadoda akhe ababezihlanganise loBhali-Peyori.
Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”
6 Khangela-ke, umuntu wabantwana bakoIsrayeli weza waletha kubafowabo umMidiyanikazi phambi kwamehlo kaMozisi laphambi kwamehlo enhlangano yonke yabantwana bakoIsrayeli, besakhala inyembezi emnyango wethente lenhlangano.
Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano.
7 Kwathi uPhinehasi, indodana kaEleyazare, indodana kaAroni umpristi, ekubona, wasukuma ephuma phakathi kwenhlangano, wathatha umkhonto esandleni sakhe,
Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake.
8 waseyilandela indoda yakoIsrayeli ethenteni, wabagwaza bobabili, indoda yakoIsrayeli lowesifazana esiswini sakhe. Yasimiswa inhlupheko kubantwana bakoIsrayeli.
Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli.
9 Lalabo abafayo ngenhlupheko babeyizinkulungwane ezingamatshumi amabili lane.
Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.
10 INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
Yehova anawuza Mose kuti,
11 UPhinehasi, indodana kaEleyazare indodana kaAroni umpristi, uphendule ulaka lwami lusuka ebantwaneni bakoIsrayeli, ngoba wayelobukhwele ngobukhwele bami phakathi kwabo; ngakho kangibaqothulanga abantwana bakoIsrayeli ngobukhwele bami.
“Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga.
12 Ngakho utsho: Khangela, ngiyamnika isivumelwano sami sokuthula.
Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye.
13 Njalo uzakuba laso, lenzalo yakhe emva kwakhe, isivumelwano sobupristi obulaphakade, ngenxa yokuthi elobukhwele ngoNkulunkulu wakhe, wabenzela abantwana bakoIsrayeli inhlawulo yokuthula.
Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”
14 Lebizo lendoda yakoIsrayeli eyatshaywayo, eyatshaywa kanye lomMidiyanikazi, lalinguZimri indodana kaSalu, isiphathamandla sendlu kayise phakathi kwabakoSimeyoni.
Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni.
15 Ibizo lowesifazana owatshaywayo, umMidiyanikazi, lalinguKozibi indodakazi kaZuri, owayeyinhloko yesizwe sendlu kayise eMidiyani.
Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.
16 INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Hluphani amaMidiyani, liwatshaye;
“Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe,
18 ngoba aliphethe njengezitha ngobuqili bawo, alikhohlisa ngodaba lukaPeyori langodaba lukaKozibi, indodakazi yesiphathamandla seMidiyani, udadewabo, owatshaywa ngosuku lwenhlupheko ngenxa yodaba lukaPeyori.
chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”