< Amanani 21 >

1 Kwathi inkosi yeAradi, umKhanani, eyayihlala eningizimu, isizwa ukuthi uIsrayeli uyeza ngendlela yabahloli, yalwa imelene loIsrayeli yathumba abanye kubo.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
2 UIsrayeli wathembisa isithembiso eNkosini wathi: Uba unikela lokunikela lababantu esandleni sami, ngizatshabalalisa imizi yabo.
Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
3 INkosi yasisizwa ilizwi likaIsrayeli, yanikela amaKhanani, wawatshabalalisa lemizi yawo; ngakho wabiza ibizo laleyondawo ngokuthi yiHorma.
Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
4 Basebesuka entabeni yeHori, ngendlela yoLwandle oluBomvu ukuze baceze ilizwe leEdoma; lomphefumulo wabantu wadinwa endleleni.
Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
5 Abantu basebekhuluma bemelene loNkulunkulu njalo bemelene loMozisi bathi: Lasenyuselani lisikhupha eGibhithe ukuze sifele enkangala? Ngoba kakulasinkwa njalo kakulamanzi, futhi umphefumulo wethu unengwa yilesisinkwa esilula.
ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
6 INkosi yasithuma inyoka ezilokutshisa phakathi kwabantu, zasezibaluma abantu, njalo kwafa abantu abanengi koIsrayeli.
Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
7 Ngakho abantu beza kuMozisi bathi: Sonile, ngoba sikhulume simelene leNkosi njalo simelene lawe; khuleka eNkosini ukuze isuse izinyoka kithi. UMozisi wasebakhulekela abantu.
Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
8 INkosi yasisithi kuMozisi: Zenzele inyoka elomlilo, uyibeke esigodweni; njalo kuzakuthi wonke olunyiweyo, nxa eyikhangela, uzaphila.
Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
9 UMozisi wasesenza inyoka yethusi, wayibeka esigodweni; kwasekusithi lapho inyoka ilume loba nguwuphi umuntu, uba ekhangele inyoka yethusi, waphila.
Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
10 Njalo abantwana bakoIsrayeli basuka bamisa inkamba eObothi.
Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
11 Basuka eObothi, bamisa inkamba eIye-Abarimi enkangala emaqondana lakoMowabi lapho okuphuma khona ilanga.
Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
12 Basuka lapho, bamisa inkamba esigodini seZeredi.
Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
13 Basuka lapho, bamisa inkamba ngale kweArinoni esenkangala ephuma emingceleni yamaAmori; ngoba iArinoni lingumngcele wakoMowabi, phakathi kweMowabi lamaAmori.
Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
14 Ngakho kuthiwa egwalweni lwezimpi zeNkosi: IWahebi eseSufa, lezifula zeArinoni,
Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
15 leliwa lezifula elehlela endaweni yeAri, lisekele umngcele wakoMowabi.
ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
16 Basebesuka lapho baya eBeri; lo ngumthombo iNkosi eyakhuluma ngawo kuMozisi yathi: Buthanisa abantu, ngizabanika-ke amanzi.
Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
17 Khona uIsrayeli wahlabela lingoma ethi: Mpompoza, mthombo! Hlabelelani kuwo,
Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
18 umthombo ezawugebhayo iziphathamandla, ezawugebhayo izikhulu zabantu, ngomnikumthetho, ngendondolo zazo. Basebesuka enkangala baya eMathana.
chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
19 Besuka eMathana baya eNahaliyeli; besuka eNahaliyeli baya eBamothi;
Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
20 besuka eBamothi esigodini esisemhlabeni wakoMowabi, engqongeni yePisiga ekhangele inkangala.
ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
21 UIsrayeli wasethuma izithunywa kuSihoni inkosi yamaAmori, esithi:
Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
22 Ake ngidabule elizweni lakho; kasiyikuphambukela emasimini loba ezivinini; kasiyikunatha amanzi omthombo; sizahamba ngomgwaqo wenkosi, size sedlule imingcele yakho.
“Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
23 Kodwa uSihoni kamvumelanga uIsrayeli ukudabula umngcele wakhe, kodwa uSihoni wabuthanisa bonke abantu bakhe, waphuma ukumelana loIsrayeli enkangala, wafika eJahazi, walwa emelene loIsrayeli.
Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
24 UIsrayeli wamtshaya ngobukhali benkemba, waba ngumnikazi welizwe lakhe kusukela eArinoni kuze kube seJaboki, kuze kube sebantwaneni bakoAmoni, ngoba umngcele wabantwana bakoAmoni wawuqinile.
Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
25 UIsrayeli wasethatha yonke le imizi; uIsrayeli wasehlala emizini yonke yamaAmori, eHeshiboni layo yonke imizana yalo.
Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
26 Ngoba iHeshiboni yayingumuzi kaSihoni inkosi yamaAmori, owayelwe emelene lenkosi yamandulo yakoMowabi, wayethethe ilizwe lonke layo esandleni sayo, kwaze kwafika eArinoni.
Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
27 Ngakho abasebenzisa izaga bathi: Wozani eHeshiboni! Umuzi kaSihoni kawakhiwe, umiswe.
Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
28 Ngoba umlilo waphuma eHeshiboni, ilangabi emzini kaSihoni, laqothula iAri loMowabi, amakhosi endawo eziphakemeyo zeArinoni.
“Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
29 Maye kuwe, Mowabi! Selibhujisiwe, bantu bakaKemoshi! Unikele amadodana akhe aba ngababaleki, lamadodakazi akhe ekuthunjweni kuSihoni, inkosi yamaAmori.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
30 Sesibatshokile; iHeshiboni ibhubhile kuze kube seDiboni; sesibachithile kuze kube seNofa, efika eMedeba.
“Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
31 UIsrayeli wasehlala elizweni lamaAmori.
“Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
32 UMozisi wathuma ukuyahlola iJazeri; basebethumba imizana yalo, baxotsha amaAmori ayehlala khona.
Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
33 Basebephenduka, benyuka ngendlela yeBashani. UOgi inkosi yeBashani wasephuma ukumelana labo, yena labantu bakhe bonke, empini eEdreyi.
Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
34 INkosi yasisithi kuMozisi: Ungamesabi; ngoba ngimnikele esandleni sakho, labantu bakhe bonke, lelizwe lakhe; njalo uzakwenza kuye njengokwenza kwakho kuSihoni inkosi yamaAmori owayehlala eHeshiboni.
Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
35 Basebemtshaya, lamadodana akhe, labantu bakhe bonke, akwaze kwasala ophilayo kuye. Badla ilifa lelizwe lakhe.
Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.

< Amanani 21 >