< Amanani 12 >

1 UMiriyamu loAroni basebekhuluma bemelene loMozisi ngenxa yowesifazana umEthiyophiyakazi owayemthethe, ngoba wayethethe umfazi umEthiyophiyakazi.
Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi.
2 Basebesithi: Kambe, iNkosi ikhulume ngoMozisi kuphela? Kayikhulumanga langathi? LeNkosi yakuzwa.
Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.
3 Njalo indoda uMozisi yayimnene kakhulu kulabo bonke abantu abaphezu kobuso bomhlaba.
(Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).
4 Khona iNkosi yahle yathi kuMozisi lakuAroni lakuMiriyamu: Phumani lobathathu lize ethenteni lenhlangano. Baphuma-ke bona bobathathu.
Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.
5 INkosi yasisehla isensikeni yeyezi, yema emnyango wethente, yabiza uAroni loMiriyamu; basebephuma bobabili.
Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo,
6 Yasisithi: Zwanini-ke amazwi ami; uba kukhona umprofethi phakathi kwenu, mina iNkosi ngizaziveza kuye ngombono, ngikhulume laye ngephupho.
Mulungu anati, “Mverani mawu anga: “Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu, ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya, ndimayankhula naye mʼmaloto.
7 Kodwa inceku yami uMozisi kanjalo, uthembekile endlini yami yonke.
Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga; Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
8 Ngikhuluma laye umlomo ngomlomo, langokubona, kungeyisikho ngemizekeliso; futhi ukhangela isimo seNkosi. Ngakho kungani belingesabi ukukhuluma limelene lenceku yami uMozisi?
Ndimayankhula naye maso ndi maso, momveka bwino osati mophiphiritsa; ndipo amaona maonekedwe a Yehova. Nʼchifukwa chiyani simunaope kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”
9 Njalo ulaka lweNkosi lwabavuthela; yasihamba.
Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.
10 Kwathi lapho iyezi lisuka phezu kwethente, khangela, uMiriyamu wayelobulephero, emhlophe njengeliqhwa elikhithikileyo. UAroni wasemkhangela uMiriyamu, khangela-ke, ulobulephero.
Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate;
11 UAroni wasesithi kuMozisi: Hawu nkosi yami, akungabeki isono phezu kwethu, okungaso senze ngobuthutha, lokungaso sonile.
ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa.
12 Ake angabi njengofileyo, othi nxa ephuma esiswini sikanina ingxenye yenyama yakhe idliwe.
Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”
13 UMozisi wasekhala eNkosini esithi: Nkulunkulu, ake umelaphe, ngiyakuncenga.
Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”
14 INkosi yasisithi kuMozisi: Uba uyise ubemkhafulele lokumkhafulela ngamathe ebusweni bakhe, ubengayikuyangeka insuku eziyisikhombisa yini? Kavalelwe ngaphandle kwenkamba insuku eziyisikhombisa; lemva kwalokho emukelwe.
Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.”
15 UMiriyamu wasevalelwa ngaphandle kwenkamba insuku eziyisikhombisa; labantu kabasukanga, waze wemukelwa uMiriyamu.
Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.
16 Lemva kwalokho abantu basuka eHazerothi, bamisa inkamba enkangala yeParani.
Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.

< Amanani 12 >