< UNehemiya 2 >
1 Kwasekusithi ngenyanga kaNisani, ngomnyaka wamatshumi amabili kaAthakisekisi inkosi, iwayini laliphambi kwakhe, ngaphakamisa iwayini nganika inkosi. Njalo ngangingakaze ngidane phambi kwayo.
Pa mwezi wa Nisani, mʼchaka cha makumi awiri cha ufumu wa Aritasasita, atabwera ndi vinyo pamaso pa mfumu ine ndinatenga vinyoyo ndi kupereka kwa mfumu. Koma ndinali ndisanakhalepo ndi nkhope yachisoni pamaso pake.
2 Inkosi yasisithi kimi: Kungani ubuso bakho budanile lokhu ungaguli? Kakusilutho ngaphandle kokudana kwenhliziyo. Ngasengisesaba kakhulukazi,
Tsono mfumu inandifunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani nkhope yako ikuoneka yachisoni pamene iwe sukudwala? Ichi si chinthu china koma chisoni cha mu mtima.” Ine ndinachita mantha kwambiri.
3 ngathi enkosini: Kayiphile inkosi kuze kube nininini! Ubuso bami bungedane ngani nxa umuzi, indawo yamangcwaba abobaba, ulunxiwa, lamasango awo eqedwe ngomlilo?
Ndinawuza mfumu kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wamuyaya! Kodi nkhope yanga ilekerenji kuoneka yachisoni pamene mzinda umene kuli manda a makolo anga, wasanduka bwinja ndipo zipata zake zinawonongedwa ndi moto?”
4 Inkosi yasisithi kimi: Kuyini okudingayo? Ngasengikhuleka kuNkulunkulu wamazulu.
Apo mfumu inandifunsa kuti, “Tsono ukufuna kundipempha chiyani?” Ndipo ine ndinapemphera kwa Mulungu Wakumwamba.
5 Ngathi enkosini: Uba kukuhle enkosini, njalo uba inceku yakho ithole umusa phambi kwakho, ngicela ukuthi ungithume koJuda emzini wamangcwaba abobaba, ukuze ngiwakhe.
Ndipo ndinayankha kuti, “Ngati amfumu chingakukondweretseni, ngati mungakomere mtima mtumiki wanune, mundilole kuti ndipite ku Yuda, ku mzinda kumene kuli manda a makolo anga kuti ndikawumangenso.”
6 Inkosi yasisithi kimi, lendlovukazi ihlezi eceleni kwayo: Uhambo lwakho luzakuba ngolwesikhathi esingakanani, ubuye nini? Ngakho kwaba kuhle phambi kwenkosi ukuthi ingithume; ngasengiyinika isikhathi esimisiweyo.
Tsono mfumu, mfumukazi itakhala pambali pake, anandifunsa kuti, “Kodi kumeneko ukakhalako masiku angati ndipo udzabwera liti?” Ndinayiwuza mfumu nthawi yake ndipo inandilola kuti ndipite.
7 Ngasengisithi enkosini: Uba kulungile enkosini kayinginike izincwadi eziya kubabusi bangaphetsheya komfula ukuze bangivumele ukudlula, ngize ngifike koJuda;
Ndipo ndinatinso kwa mfumu, “Ngati zikondweretse mfumu, mundipatse makalata oti ndikapereke kwa abwanamkubwa a ku chigawo cha Patsidya pa Yufurate, kuti akandilole kudutsa mwamtendere mpaka nditakafika ku Yuda.
8 lencwadi eya kuAsafi, umphathi wegusu inkosi elalo, ukuthi anginike izigodo zokwenza imigubazi yamasango lesigodlo esiseduze lendlu, lezomduli womuzi, lezendlu engizangena kiyo. Inkosi yanginika njengokwesandla esihle sikaNkulunkulu wami phezu kwami.
Mundipatsenso kalata yokapereka kwa Asafu woyangʼanira nkhalango ya mfumu, kuti akandipatse mitengo yokapangira mitanda ya zipata za nsanja yoteteza Nyumba ya Mulungu, mitanda ya khoma la mzinda ndi ya nyumba yokhalamo ine.” Mfumu indipatse zomwe ndinapempha popeza Yehova wokoma mtima anali nane.
9 Ngasengifika kubabusi ngaphetsheya komfula, ngabanika incwadi zenkosi. Inkosi yayithume-ke lami induna zebutho labagadi bamabhiza.
Choncho ndinanyamuka ulendo wanga ndipo ndinafika kwa abwanamkubwa a chigawo cha Patsidya pa Yufurate ndipo ndinawapatsa makalata a mfumu. Mfumu nʼkuti itatumiza akulu ankhondo ndi okwera pa akavalo kuti atsagane nane.
10 Lapho uSanibhalathi umHoroni loTobiya inceku, umAmoni, besizwa, kwabacunula ngokucunula okukhulu ukuthi umuntu ufikile ukudingela abantwana bakoIsrayeli okuhle.
Sanibalati wa ku Horoni ndi Tobiya wa ku Amoni atamva zimenezi, iwo anayipidwa kwambiri kuti wina wabwera kudzachitira zabwino Aisraeli.
11 Ngafika-ke eJerusalema, ngaba lapho insuku ezintathu.
Ndinafika ku Yerusalemu, ndipo ndinakhala kumeneko masiku atatu.
12 Ngasengisukuma ebusuku, mina lamadoda amalutshwana elami; kangitshelanga muntu lokho uNkulunkulu wami ayekufake enhliziyweni yami ukuthi ngikwenzele iJerusalema. Futhi kwakungelanyamazana kanye lami ngaphandle kwenyamazana engangiyigadile.
Sindinawuze munthu aliyense za zimene Yehova anayika mu mtima mwanga kuti ndichitire mzinda wa Yerusalemu. Choncho ndinanyamuka usiku pamodzi ndi anthu ena owerengeka. Ndinalibe bulu wina aliyense kupatula amene ndinakwerapo.
13 Ngasengiphuma ebusuku ngesango lesigodi, ngaqonda emthonjeni womgobho lesangweni lomquba, ngihlola imiduli yeJerusalema eyayidilikile lamasango ayo ayeqedwe ngomlilo.
Ndinatuluka usiku podzera ku Chipata cha ku Chigwa ndi kuyenda kupita ku Chitsime cha Chirombo Chamʼmadzi mpaka ku Chipata cha Zinyalala. Ndinayangʼana makoma a Yerusalemu, amene anagwetsedwa, ndi zipata zake, zimene zinawonongedwa ndi moto.
14 Ngasengisedlulela esangweni lomthombo lechibini lenkosi; kodwa kwakungelandawo yenyamazana ukwedlula ngaphansi kwami.
Kenaka ndinapita ku Chipata cha Kasupe ndi ku Dziwe la Mfumu. Koma panalibe malo okwanira akuti bulu wanga adutse.
15 Ngasengisenyuka ngesifula ebusuku ngihlola umduli; ngaphenduka, ngangena ngesango lesigodi, ngabuyela.
Kotero usikuwo ndinapita ku chigwa, ndikuyangʼana khomalo. Pomaliza ndinabwerera ndi kukalowanso mu mzinda kudzera ku Chipata cha ku Chigwa.
16 Lababusi babengazi lapho engangiye khona lokuthi ngenzani. Kuze kube khathesi-ke ngangingatshelanga amaJuda labapristi leziphathamandla lezinduna labanye ababesenza umsebenzi.
Akuluakulu sanadziwe kumene ndinapita kapena zimene ndimachita, chifukwa pa nthawiyi nʼkuti ndisananene kalikonse kwa Ayuda kapena ansembe, anthu olemekezeka kapena akuluakulu, kapena wina aliyense amene anali woyenera kugwira ntchitoyi.
17 Ngasengisithi kibo: Liyabona inhlupheko esikiyo ukuthi iJerusalema ilunxiwa lamasango ayo atshiswe ngomlilo. Wozani sakhe umduli weJerusalema ukuze singabe sisaba lihlazo.
Ndinawawuza kuti, “Inu mukuona mavuto amene tili nawo. Mukuona kuti mzinda wa Yerusalemu wasanduka bwinja ndipo zipata zake zatenthedwa ndi moto. Tsono tiyeni timangenso makoma a Yerusalemu ndipo sitidzachitanso manyazi.”
18 Ngasengibatshela ngesandla sikaNkulunkulu wami esasisihle phezu kwami, futhi lamazwi enkosi eyayiwakhulume kimi. Basebesithi: Asisukumeni, sakhe. Ngakho baqinisa izandla zabo ngokuhle.
Ndinawawuza za mmene Yehova Mulungu wanga anandichitira zabwino ndiponso mawu amene mfumu inandiwuza. Tsono anati, “Tiyeni tiyambenso kumanga.” Kotero analimbitsana mtima kuti ayambenso ntchito yabwinoyi.
19 Lapho uSanibhalathi umHoroni loTobiya inceku, umAmoni, loGeshema umArabhiya besizwa basihleka usulu, baseyisa bathi: Iyini linto eliyenzayo? Liyayivukela inkosi yini?
Koma Sanibalati wa ku Horoni, Tobiya wa ku Amoni ndi Gesemu Mwarabu atamva zimenezi, anatiseka ndi kutinyoza. Iwo anafunsa kuti, “Kodi muti ndi chiyani chimene mukuchitachi? Kodi mufuna kuwukira mfumu?”
20 Ngasengibabuyisela impendulo ngathi kibo: UNkulunkulu wamazulu yena uzasiphumelelisa; lathi inceku zakhe sizasukuma sakhe; kodwa lina kalilasabelo lelungelo lesikhumbuzo eJerusalema.
Koma ndinawayankha kuti, “Mulungu Wakumwamba atithandiza kuti zinthu zitiyendere bwino. Ife antchito ake tiyambapo kumanga. Koma inu mulibe gawo lanu muno mu Yerusalemu. Mulibe chokuyenerezani kulandira malo ano. Mulibenso chilichonse muno chokumbutsa za inu.”