< UMalaki 3 >

1 Khangelani, ngithuma isithunywa sami, esizalungisa indlela phambi kwami; leNkosi eliyidingayo izafika masinyane ethempelini layo, ngitsho isithunywa sesivumelwano elithokoza ngaso; khangela siyeza, itsho iNkosi yamabandla.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
2 Kodwa ngubani ongalumela usuku lokuza kwaso, njalo ngubani ongema ekubonakaleni kwaso? Ngoba sinjengomlilo womcwengi wegolide, lanjengesepa yomwatshi.
Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
3 Sizahlala njengomcwengi lomhlambululi wesiliva, sihlambulule amadodana kaLevi, siwacwenge njengegolide lanjengesiliva; ukuze asondeze iminikelo ngokulunga eNkosini.
Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
4 Lapho umnikelo wakoJuda loweJerusalema uzakuba mnandi eNkosini njengensukwini zendulo, lanjengeminyakeni yakuqala.
ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
5 Njalo ngizasondela kini ngokwahlulela; ngibe ngumfakazi ophangisayo ngimelene labathakathi, ngimelene lezifebe, ngimelene labafungi bamanga, ngimelene labacindezeli bamaholo abaqhatshiweyo, umfelokazi, lentandane, labasunduzela abezizweni eceleni, njalo abangangesabiyo, itsho iNkosi yamabandla.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
6 Ngoba ngiyiNkosi, kangiphenduki; ngakho lina madodana kaJakobe kaliqedwa.
“Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
7 Ngitsho kusukela ensukwini zaboyihlo liphambukile ezimisweni zami, kalizigcinanga. Buyelani kimi, lami ngizabuyela kini, itsho iNkosi yamabandla. Kanti lithi: Sizabuyela ngani?
Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
8 Umuntu angamphanga yini uNkulunkulu? Kanti lina lingiphangile. Kodwa lithi: Sikuphange ngani? Ngokwetshumi langomnikelo.
“Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
9 Liqalekisiwe ngesiqalekiso, ngoba lingiphangile, lesisizwe sonke.
Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
10 Lethani konke okwetshumi esiphaleni ukuze kube lokudla endlini yami. Lingihlole-ke khathesi kukho, itsho iNkosi yamabandla, uba ngingayikulivulela amawindi amazulu, ngilithululele isibusiso kuze kungabi lendawo eyaneleyo.
Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
11 Ngizakhuza odlayo ngenxa yenu, njalo kayikulichithela izithelo zomhlabathi; levini kaliyikulibozisela ensimini, itsho iNkosi yamabandla.
Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 Njalo zonke izizwe zizakuthi libusisiwe, ngoba lina lizakuba yilizwe elithokozisayo, itsho iNkosi yamabandla.
“Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
13 Amazwi enu abelukhuni emelene lami, itsho iNkosi. Kanti lithi: Sikhulumeni simelene lawe?
Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
14 Lithe: Kuyize ukukhonza uNkulunkulu. Njalo kuyinzuzo bani ukuthi sigcine imfanelo yakhe, lokuthi sihambe sikwezimnyama phambi kweNkosi yamabandla?
“Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
15 Khathesi-ke sithi abaziqhenyayo babusisiwe; yebo, labo abenza inkohlakalo bayakhiwa; yebo balinga uNkulunkulu, baphephe.
Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
16 Khona labo abayesabayo iNkosi bakhulumisana; njalo iNkosi yalalela, yezwa; logwalo lwesikhumbuzo lwalotshwa phambi kwayo ngabo abayesabayo iNkosi, langalabo abazindla ngebizo layo.
Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
17 Njalo bazakuba ngabami, itsho iNkosi yamabandla, ngalolosuku engizakwenza ngalo okuligugu kwami, njalo ngizabayekela njengendoda eyekela indodana yayo eyisebenzelayo.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
18 Beselibuya libona umehluko phakathi kolungileyo lomubi, phakathi kokhonza uNkulunkulu lalowo ongamkhonziyo.
Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”

< UMalaki 3 >