< Abahluleli 8 >
1 Amadoda akoEfrayimi asesithi kuye: Iyini linto oyenze kithi ukuthi awusibizanga nxa usiyakulwa lamaMidiyani? Amsola ngamandla.
Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.
2 Wasesithi kiwo: Ngenzeni khathesi uba kulinganiswa lokwenu? Ukukhothozwa kwezithelo zevini koEfrayimi kakukuhle yini kulesivuno sevini sakoAbiyezeri?
Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita?
3 UNkulunkulu unikele esandleni senu iziphathamandla zeMidiyani, uOrebi loZebi; ngangingenzani njengani? Kwasekudeda kuye ukuthukuthela kwabo lapho ekhuluma lelilizwi.
Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.
4 Lapho uGidiyoni efika eJordani wachapha, yena lamadoda angamakhulu amathathu ayelaye, bediniwe kodwa bexotsha.
Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo.
5 Wasesithi emadodeni eSukothi: Ake liphe abantu abangilandelayo amaqebelengwana ezinkwa, ngoba badiniwe, ngixotshana loZeba loZalimuna amakhosi eMidiyani.
Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”
6 Lenduna zeSukothi zathi: Intende yesandla sikaZeba loZalimuna isisesandleni sakho yini, ukuthi siphe ibutho lakho isinkwa?
Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”
7 UGidiyoni wasesithi: Ngakho nxa iNkosi isinikele uZeba loZalimuna esandleni sami, ngizabhula inyama yenu ngameva enkangala langokhula oluhlabayo.
Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”
8 Wasesenyuka lapho waya ePenuweli, wakhuluma labo ngokufananayo; lamadoda ePenuweli amphendula njengamadoda eSukothi emphendulile.
Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja.
9 Wasekhuluma futhi emadodeni ePenuweli esithi: Ekubuyeni kwami ngokuthula ngizadiliza lo umphotshongo.
Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”
10 Njalo uZeba loZalimuna babeseKarikori lenkamba yabo ilabo, phose inkulungwane ezilitshumi lanhlanu, bonke ababesele ebuthweni lonke labantwana bempumalanga, ngoba ababewile babengamadoda azinkulungwane ezilikhulu lamatshumi amabili abahwatsha inkemba.
Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000.
11 UGidiyoni wasesenyuka ngendlela yabahlala emathenteni empumalanga kweNoba leJogibeha, wayitshaya inkamba, ngoba inkamba yayilibele.
Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera.
12 UZeba loZalimuna basebebaleka, wasexotshana labo, wathumba amakhosi amabili eMidiyani, uZeba loZalimuna, wethusa inkamba yonke.
Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.
13 Lapho uGidiyoni indodana kaJowashi esebuya evela empini phambi kokuphuma kwelanga,
Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi.
14 wabamba ijaha emadodeni eSukothi, walibuza; laselimbhalela iziphathamandla zeSukothi labadala bayo, amadoda angamatshumi ayisikhombisa lesikhombisa.
Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti.
15 Wasefika emadodeni eSukothi, wathi: Khangelani oZeba loZalimuna elalingiklolodela ngabo lisithi: Intende yesandla sikaZeba loZalimuna isisesandleni sakho yini, ukuthi siphe amadoda akho asediniwe isinkwa?
Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’”
16 Wasethatha abadala bomuzi, lameva enkangala lokhula oluhlabayo, wenza amadoda eSukothi aqedisise ngawo.
Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo.
17 Lomphotshongo wePenuweli wawudiliza, wabulala amadoda omuzi.
Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.
18 Wasesithi kuZeba lakuZalimuna: Ngamadoda anjani elawabulala eThabhori? Basebesithi: Njengawe babenjalo, ngulowo njengesimo sendodana yenkosi.
Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?” Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”
19 Wasesithi: Babengabafowethu, abantwana bakamama. Kuphila kukaJehova, uba belibayekele baphila, bengingayikulibulala.
Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.”
20 Wasesithi kuJetheri izibulo lakhe: Sukuma ubabulale. Kodwa umfana kayihwatshanga inkemba yakhe, ngoba wayesesaba ngoba esesengumfana.
Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.
21 UZeba loZalimuna basebesithi: Sukuma wena uwele phezu kwethu, ngoba njengoba injalo indoda, anjalo amandla ayo. Wasesukuma uGidiyoni wabulala uZeba loZalimuna. Wasethatha izinyangana ezazisentanyeni zamakamela abo.
Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.
22 Amadoda akoIsrayeli asesithi kuGidiyoni: Sibuse, wena-ke, lendodana yakho, lendodana yendodana yakho, ngoba usisindisile esandleni samaMidiyani.
Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”
23 Kodwa uGidiyoni wathi kibo: Mina kangiyikulibusa, lendodana yami kayiyikulibusa; iNkosi izalibusa.
Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.”
24 UGidiyoni wasesithi kibo: Ake ngicele isicelo kini; nginikani ngamunye icici lempango yakhe. Ngoba babelamacici egolide, ngoba babengamaIshmayeli.
Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).
25 Basebesithi: Sizanika lokunika. Basebesendlala isembatho, baphosela lapho ngamunye icici lempango yakhe.
Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha.
26 Lesisindo samacici egolide ayewacelile sasingamashekeli egolide ayinkulungwane lamakhulu ayisikhombisa, ngaphandle kwezinyangana, leziceciso ezilengayo, lezembatho eziyibubende ezazisemakhosini eMidiyani, langaphandle kwamaketane ayesezintanyeni zamakamela awo.
Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo.
27 UGidiyoni wasesenza i-efodi ngakho, wayibeka emzini wakhe, eOfira. LoIsrayeli wonke waphinga lapho ngokuyilandela; yasisiba ngumjibila kuGidiyoni lendlu yakhe.
Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.
28 Ngokunjalo amaMidiyani ehliselwa phansi phambi kwabantwana bakoIsrayeli, kawaphindanga aphakamisa ikhanda lawo. Lelizwe laba lokuthula iminyaka engamatshumi amane ensukwini zikaGidiyoni.
Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.
29 UJerubali indodana kaJowashi wayahlala-ke endlini yakhe.
Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo.
30 Njalo uGidiyoni wayelamadodana angamatshumi ayisikhombisa aphuma okhalweni lwakhe, ngoba wayelabafazi abanengi.
Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri.
31 Lomfazi wakhe omncane owayeseShekema laye wamzalela indodana, wayitha ibizo lokuthi nguAbhimeleki.
Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki.
32 UGidiyoni indodana kaJowashi wasesifa eseluphele kuhle, wangcwatshelwa engcwabeni likaJowashi uyise, eOfira yamaAbiyezeri.
Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.
33 Kwasekusithi lapho uGidiyoni esefile, abantwana bakoIsrayeli baphenduka, baphinga ngokulandela oBhali, bazimisela uBhali-Berithi waba ngunkulunkulu.
Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo.
34 Njalo abantwana bakoIsrayeli kabayikhumbulanga iNkosi uNkulunkulu wabo eyabophula esandleni sezitha zabo zonke inhlangothi zonke.
Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse.
35 Kabenzanga umusa endlini kaJerubali, onguGidiyoni, njengakho konke okuhle akwenza kuIsrayeli.
Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.