< Abahluleli 2 >

1 Ingilosi yeNkosi yasisenyuka isuka eGiligali isiya eBokimi, yathi: Ngalenyusa lisuka eGibhithe, ngaliletha elizweni engalifungela oyihlo, njalo ngathi: Kangiyikwephula isivumelwano sami lani kuze kube sephakadeni.
Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
2 Lani-ke kaliyikwenza isivumelwano labahlali balelilizwe, lizadiliza amalathi abo. Kodwa kalililalelanga ilizwi lami. Kuyini lokhu elikwenzileyo?
ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
3 Ngakho lami ngathi: Kangiyikuzixotsha elifeni phambi kwenu, kodwa zizakuba njengameva enhlangothini zenu, labonkulunkulu bazo babe ngumjibila kini.
Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
4 Kwasekusithi lapho ingilosi yeNkosi isikhulume lamazwi kubo bonke abantwana bakoIsrayeli, abantu baphakamisa ilizwi labo bakhala inyembezi.
Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
5 Basebebiza ibizo laleyondawo ngokuthi yiBokimi, bayihlabela iNkosi lapho.
ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
6 Kwathi uJoshuwa esebayekele abantu bahamba, abantwana bakoIsrayeli bahamba, ngulowo lalowo waya elifeni lakhe ukudla ilifa lelizwe.
Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
7 Abantu basebeyikhonza iNkosi kuzo zonke izinsuku zikaJoshuwa, lazo zonke izinsuku zabadala abasala bephila emva kukaJoshuwa, ababewubonile wonke umsebenzi omkhulu weNkosi eyayiwenzele uIsrayeli.
Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
8 UJoshuwa indodana kaNuni, inceku yeNkosi, wafa-ke, eleminyaka elikhulu letshumi.
Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
9 Basebemngcwabela emngceleni welifa lakhe eThiminathi-Heresi entabeni yakoEfrayimi, enyakatho kwentaba iGahashi.
Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
10 Njalo lalesosizukulwana sabuthelwa kuboyise. Kwasekusukuma esinye isizukulwana emva kwabo esasingayazi iNkosi njalo lomsebenzi eyayiwenzele uIsrayeli.
Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
11 Abantwana bakoIsrayeli basebesenza okubi emehlweni eNkosi, bakhonza oBhali.
Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
12 Batshiya iNkosi, uNkulunkulu waboyise, eyabakhupha elizweni leGibhithe, balandela abanye onkulunkulu, kubonkulunkulu bezizwe ezazibazingelezele, bakhothama kibo, bayithukuthelisa iNkosi.
Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
13 Bayidela iNkosi, bakhonza uBhali laboAshitarothi.
Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
14 Ngakho ulaka lweNkosi lwavutha kuIsrayeli, yabanikela esandleni sabaphangi ababaphangayo; yabathengisa esandleni sezitha zabo inhlangothi zonke, ukuze bangabe besaba lakho ukuma phambi kwazo.
Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
15 Loba bephuma besiya ngaphi, isandla seNkosi samelana labo ngokubi, njengokutsho kweNkosi lanjengokufunga kweNkosi kibo, njalo bacindezeleka kakhulu.
Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
16 INkosi yasimisa abahluleli ababophula esandleni salabo ababaphangayo.
Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
17 Kanti kababalalelanga labahluleli babo, kodwa baphinga ngokulandela abanye onkulunkulu, bakhothama kibo; baphambuka masinyane endleleni oyise ababehamba kuyo, belalela imilayo yeNkosi. Bona kabenzanga njalo.
Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
18 Lalapho iNkosi ibamisela abahluleli, iNkosi yayilomahluleli, yabophula esandleni sezitha zabo zonke izinsuku zikamahluleli; ngoba iNkosi yazisola ngenxa yokububula kwabo ngenxa yalabo ababacindezelayo lababahlukuluzayo.
Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
19 Kwasekusithi ekufeni kukamahluleli, babuyela emuva baxhwala okwedlula oyise, ngokulandela abanye onkulunkulu, ngokubakhonza langokubakhothamela; kabalahlanga okwemisebenzi yabo lokwendlela yabo yenkani.
Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
20 Ngakho ulaka lweNkosi lwavutha kuIsrayeli, yathi: Ngoba lesisizwe seqe isivumelwano sami engasilaya oyise, kasilalelanga ilizwi lami,
Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
21 lami kangisayikuxotsha loba ngubani elifeni phambi kwabo ezizweni uJoshuwa azitshiya ekufeni kwakhe,
Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
22 ukuze ngihlole ngazo uIsrayeli ukuthi bazagcina yini indlela yeNkosi ukuhamba kuyo njengaboyise bayigcina, kumbe hatshi.
Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
23 Ngakho iNkosi yaziyekela lezozizwe, ukuze ingazixotshi elifeni masinyane, njalo kayizinikelanga esandleni sikaJoshuwa.
Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.

< Abahluleli 2 >