< Abahluleli 10 >

1 Emva kukaAbhimeleki kwasekuvela uThola indodana kaPhuwa indodana kaDodo, indoda yakoIsakari ukukhulula uIsrayeli; wayehlala eShamiri entabeni yakoEfrayimi.
Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
2 Wasesahlulela uIsrayeli iminyaka engamatshumi amabili lantathu. Wafa, wangcwatshelwa eShamiri.
Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
3 Lemva kwakhe kwavela uJayiri umGileyadi, wahlulela uIsrayeli iminyaka engamatshumi amabili lambili.
Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
4 Wayelamadodana angamatshumi amathathu agada amathole abobabhemi angamatshumi amathathu, elemizi engamatshumi amathathu, abayithi yiHavothi-Jayiri kuze kube lamuhla, eselizweni leGileyadi.
Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
5 UJayiri wasesifa, wangcwatshelwa eKamoni.
Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
6 Abantwana bakoIsrayeli basebebuya besenza okubi emehlweni eNkosi, bakhonza oBhali laboAshitarothi, labonkulunkulu beSiriya labonkulunkulu beSidoni labonkulunkulu bakoMowabi labonkulunkulu babantwana bakoAmoni labonkulunkulu bamaFilisti; bayitshiya iNkosi, kabaze bayikhonza.
Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
7 Ulaka lweNkosi lwaselumvuthela uIsrayeli, yabathengisa ezandleni zamaFilisti lezandleni zabantwana bakoAmoni.
Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
8 Asebachitha abacindezela abantwana bakoIsrayeli ngalowomnyaka - iminyaka elitshumi leyisificaminwembili, bonke abantwana bakoIsrayeli ababengaphetsheya kweJordani elizweni lamaAmori eliseGileyadi.
Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
9 Njalo abantwana bakoAmoni bachapha iJordani ukuze balwe ngitsho bemelene loJuda njalo bemelene loBhenjamini bemelene lendlu kaEfrayimi; ngalokho uIsrayeli wacindezeleka kakhulu.
Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
10 Abantwana bakoIsrayeli basebekhala eNkosini besithi: Sonile kuwe, njalo ngoba sitshiyile uNkulunkulu wethu, sasesikhonza oBhali.
Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
11 INkosi yasisithi ebantwaneni bakoIsrayeli: Kangilikhululanga yini kumaGibhithe lakumaAmori lakubantwana bakoAmoni lakumaFilisti?
Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
12 AmaSidoni lawo lamaAmaleki lamaMahoni alicindezela, laselikhala kimi, ngalikhulula esandleni sawo.
Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
13 Kanti lina lingitshiyile lakhonza abanye onkulunkulu; ngakho kangisayikulikhulula.
Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
14 Hambani liyekhala kubonkulunkulu elibakhethileyo; kabalikhulule bona ngesikhathi sokuhlupheka kwenu.
Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
15 Abantwana bakoIsrayeli-ke bathi eNkosini: Sonile; yenza wena kithi njengakho konke okuhle emehlweni akho; kuphela sikhulule, siyakuncenga, lamuhla.
Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
16 Basebesusa onkulunkulu bezizweni phakathi kwabo, bakhonza iNkosi; umphefumulo wayo wasudabuka ngohlupho lukaIsrayeli.
Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
17 Kwasekubizelwa ndawonye abantwana bakoAmoni, bamisa inkamba eGileyadi, labantwana bakoIsrayeli babuthana bamisa inkamba eMizipa.
Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
18 Labantu, iziphathamandla zeGileyadi, bathi omunye komunye: Ngubani umuntu ozaqala ukulwa emelene labantwana bakoAmoni? Uzakuba yinhloko phezu kwabo bonke abahlali beGileyadi.
Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”

< Abahluleli 10 >