< UJoshuwa 1 >

1 Kwasekusithi emva kokufa kukaMozisi inceku yeNkosi, iNkosi yakhuluma kuJoshuwa indodana kaNuni, inceku kaMozisi, isithi:
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 UMozisi inceku yami usefile; ngakho-ke sukuma uchaphe le iJordani, wena labo bonke lababantu, liye elizweni engibanika lona, ebantwaneni bakoIsrayeli.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Yonke indawo lapho ingaphansi yonyawo lwenu ezanyathela khona ngilinike yona, njengokutsho kwami kuMozisi.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 Kusukela enkangala lale iLebhanoni kuze kufike emfuleni omkhulu, umfula iYufrathi, ilizwe lonke lamaHethi, njalo kufike elwandle olukhulu lapho okutshona khona ilanga, kuzakuba ngumngcele wenu.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 Kakulamuntu ozakuma phambi kwakho zonke izinsuku zempilo yakho. Njengalokhu ngangiloMozisi, ngizakuba lawe; kangiyikukutshiya, kangiyikukulahla.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 Qina, ume isibindi, ngoba wena uzakwenza lababantu badle ilifa lelizwe engalifungela oyise ukubanika lona.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Kuphela qina, ube lesibindi esikhulu, ukugcina ukwenza ngokomlayo wonke uMozisi inceku yami akulaya wona; ungaphambuki kuwo uye ngakwesokunene loba ngakwesokhohlo, ukuze uphumelele loba ngaphi lapho oya khona.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Ugwalo lwalumlayo lungasuki emlonyeni wakho, kodwa uzindle kuwo emini lebusuku, ukuze uqaphele ukwenza njengakho konke okubhaliweyo kulo, ngoba khona uzakwenza indlela yakho iphumelele, ubusuphumelela.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 Kangikulayanga yini? Qina, ume isibindi; ungesabi, ungatshaywa luvalo, ngoba iNkosi uNkulunkulu wakho ilawe loba ngaphi lapho oya khona.
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 UJoshuwa waselaya izinduna zabantu, esithi:
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 Dabulani phakathi kwenkamba lilaye abantu lithi: Zilungiseleni umphako, ngoba kusesezinsuku ezintathu lizachapha le iJordani, ukuze lingene lidle ilifa lelizwe iNkosi uNkulunkulu wenu elinika lona ukuthi lidle ilifa lalo.
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 UJoshuwa wasekhuluma kwabakoRubeni labakoGadi lengxenye yesizwe sakoManase esithi:
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 Khumbulani ilizwi uMozisi inceku yeNkosi alilaya ngalo esithi: INkosi uNkulunkulu wenu iyaliphumuza, ilinika lelilizwe.
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Omkenu, abantwanyana benu, lezifuyo zenu kuzahlala elizweni uMozisi alinika lona nganeno kweJordani; kodwa lina lizachapha lihlomile phambi kwabafowenu, wonke amaqhawe alamandla, libasize,
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 iNkosi ize iphumuze abafowenu njengani, labo njalo badle ilifa lelizwe iNkosi uNkulunkulu wenu ebanika lona. Lizabuyela-ke elizweni lelifa lenu, lidle ilifa lalo, uMozisi inceku yeNkosi alinika lona, nganeno kweJordani, empumalanga.
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 Basebemphendula uJoshuwa besithi: Konke osilaya khona sizakwenza, laloba ngaphi lapho ozasithuma khona sizahamba.
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 Njengakho konke esamlalela uMozisi ngakho, ngokunjalo sizakulalela. Kuphela iNkosi uNkulunkulu wakho ibe lawe njengoba yayiloMozisi.
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Wonke umuntu ozavukela umlomo wakho, angalaleli amazwi akho, kukho konke omlaya khona, uzabulawa. Kuphela qina, ume isibindi.
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

< UJoshuwa 1 >