< UJoshuwa 7 >
1 Kodwa abantwana bakoIsrayeli baphambuka ngesiphambeko ngokuqalekisiweyo. Ngoba uAkani indodana kaKarmi indodana kaZabidi indodana kaZera owesizwe sakoJuda wathatha kokuqalekisiweyo; ulaka lweNkosi lwaselubavuthela abantwana bakoIsrayeli.
Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
2 UJoshuwa wasethuma abantu besuka eJeriko besiya eAyi eliseduze leBeti-Aveni empumalanga kweBhetheli, wakhuluma kibo esithi: Yenyukani liyehlola ilizwe. Abantu basebesenyuka bayihlola iAyi.
Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
3 Basebebuyela kuJoshuwa bathi kuye: Kakungenyuki bonke abantu; kakwenyuke phose amadoda azinkulungwane ezimbili loba phose amadoda azinkulungwane ezintathu ukutshaya iAyi. Ungadinisi bonke abantu ngokuya khona, ngoba balutshwana.
Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
4 Kwasekusenyukela khona abavela ebantwini amadoda aphosa abe zinkulungwane ezintathu; abaleka phambi kwamadoda eAyi.
Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
5 Lamadoda eAyi atshaya phose amadoda angamatshumi amathathu lesithupha, axotshana lawo phambi kwesango aze afika eShebarimi, awatshayela ekwehleni. Ngakho inhliziyo yabantu yancibilika yaba ngamanzi.
Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
6 UJoshuwa wasedabula izigqoko zakhe, wathi mbo ngobuso emhlabathini phambi komtshokotsho weNkosi kwaze kwahlwa, yena labadala bakoIsrayeli, bathela uthuli emakhanda abo.
Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
7 UJoshuwa wasesithi: Maye Nkosi Jehova! Ubachaphiseleni lokubachaphisa lababantu iJordani ukusinikela esandleni samaAmori ukusibhubhisa? Kungathi ngabe seneliswa sahlala ngaphetsheya kweJordani!
Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
8 O Nkosi, ngizakuthini, emva kokuthi uIsrayeli esephendule intamo ezitheni zakhe?
Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
9 Ngoba amaKhanani labo bonke abakhileyo elizweni bazakuzwa, basihanqe, baliqume ibizo lethu lisuke emhlabeni. Pho, uzalenzelani ibizo lakho elikhulu?
Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
10 INkosi yasisithi kuJoshuwa: Sukuma wena, uweleni kanje ngobuso bakho?
Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
11 UIsrayeli wonile; njalo baseqile isivumelwano sami engabalaya sona, bathethe futhi kokuqalekisiweyo, njalo bebile, baqamba amanga futhi, yebo bakubekile empahleni zabo.
Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
12 Ngalokho abantwana bakoIsrayeli babengelakuma phambi kwezitha zabo, baphendula umhlana phambi kwezitha zabo, ngoba beqalekisiwe. Kangisayikuba lani uba lingabhubhisi okuqalekisiweyo phakathi kwenu.
Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
13 Sukuma, ngcwelisa abantu, uthi: Zingcweliseleleni ikusasa; ngoba itsho njalo iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli: Kukhona okuqalekisiweyo phakathi kwakho, Israyeli; ungeke ume phambi kwezitha zakho lize likhuphe okuqalekisiweyo phakathi kwenu.
“Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
14 Ngakho ekuseni lizasondezwa ngezizwe zenu; kuzakuthi-ke isizwe iNkosi ezasibamba sizasondela ngensendo, losendo iNkosi ezalubamba luzasondela ngezindlu, lendlu iNkosi ezayibamba izasondela ngabantu.
“Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
15 Kuzakuthi-ke lowo ozabanjwa lokuqalekisiweyo uzatshiswa ngomlilo, yena lakho konke alakho, ngoba eqe isivumelwano seNkosi, langoba enze ubuphukuphuku koIsrayeli.
Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
16 UJoshuwa wasevuka ekuseni kakhulu, wenza uIsrayeli wasondela ngezizwe zakhe; lesizwe sakoJuda sabanjwa;
Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
17 wasesenza usendo lwakoJuda lusondele, wabamba usendo lwakoZera; wenza usendo lwakoZera lusondele ngabantu; uZabidi wasebanjwa;
Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
18 wasesenza indlu yakhe isondele ngabantu; uAkani, indodana kaKarmi, indodana kaZabidi, indodana kaZera, owesizwe sakoJuda, wasebanjwa.
Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
19 UJoshuwa wasesithi kuAkani: Ndodana yami, ake unike iNkosi udumo, uNkulunkulu wakoIsrayeli, uvume kuye; ake ungitshele lokho okwenzileyo, ungangifihleli.
Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
20 UAkani wasephendula uJoshuwa wathi: Isibili mina ngonile eNkosini, uNkulunkulu wakoIsrayeli. Ngokunje langokunje ngikwenzile.
Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
21 Kwathi ngibona phakathi kwempango isembatho seBhabhiloni esihle esisodwa, lamashekeli esiliva angamakhulu amabili, lolimi lwegolide olulodwa osisindo salo singamashekeli angamatshumi amahlanu, ngakuhawukela, ngakuthatha, khangela-ke, kuthukuziwe emhlabathini phakathi kwethente lami, lesiliva singaphansi kwakho.
Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
22 UJoshuwa wasethuma izithunywa, zagijima zaya ethenteni, khangela-ke, kwakufihliwe ethenteni lakhe, lesiliva singaphansi kwakho.
Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
23 Bakukhupha phakathi kwethente, bakuletha kuJoshuwa lebantwaneni bonke bakoIsrayeli, bakuthululela phambi kweNkosi.
Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
24 UJoshuwa loIsrayeli wonke ekanye laye basebemthatha uAkani indodana kaZera, lesiliva, lesembatho, lolimi lwegolide, lamadodana akhe, lamadodakazi akhe, lenkabi zakhe, labobabhemi bakhe, lezimvu zakhe, lethente lakhe, lakho konke ayelakho, bakwenyusela esihotsheni seAkori.
Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
25 UJoshuwa wasesithi: Usihlupheleni? INkosi izakuhlupha lamuhla. LoIsrayeli wonke wamkhanda ngamatshe; babatshisa ngomlilo, babakhanda ngamatshe.
Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
26 Bamisa phezu kwakhe inqwaba enkulu yamatshe kuze kube lamuhla. Ngalokho iNkosi yaphenduka ekuvutheni kolaka lwayo. Ngakho ibizo laleyondawo labizwa ngokuthi yisihotsha seAkori, kuze kube lamuhla.
Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.