< UJoshuwa 23 >

1 Kwasekusithi emva kwensuku ezinengi emva kokuthi iNkosi isimphumuzile uIsrayeli ezitheni zonke zabo inhlangothi zonke, loJoshuwa wayesemdala elensuku ezinengi,
Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri.
2 uJoshuwa wabiza uIsrayeli wonke, abadala babo, lenhloko zabo, labahluleli babo, lenduna zabo, wathi kubo: Mina sengimdala ngilensuku ezinengi.
Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri.
3 Lina selibonile konke iNkosi uNkulunkulu wenu ekwenzileyo kulezizizwe zonke ngenxa yenu, ngoba iNkosi uNkulunkulu wenu yiyo elilweleyo.
Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo.
4 Bonani, ngilabele ngenkatho lezizizwe eziseleyo zibe yilifa lezizwe zenu, kusukela eJordani, lazo zonke izizwe engiziqumileyo, ngitsho kuze kube selwandle olukhulu lapho okutshona khona ilanga.
Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa.
5 INkosi uNkulunkulu wenu izazixotsha-ke phambi kwenu, izixotshe elifeni phambi kwenu, njalo lizakudla ilifa lelizwe, njengalokho iNkosi uNkulunkulu wenu ikhulumile kini.
Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.
6 Ngakho qinani kakhulu ukugcina lokwenza konke okubhaliweyo egwalweni lomlayo kaMozisi, ukuze lingaphambuki kuwo liye ngakwesokunene loba ngakwesokhohlo,
“Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo.
7 ukuze lingangeni kulezi izizwe, lezi ezisele lani, lingaphathi ibizo labonkulunkulu bazo, lingafungisi ngabo, lingabakhonzi, lingakhothami kubo,
Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira.
8 kodwa linamathele eNkosini uNkulunkulu wenu njengoba lenzile kuze kube lamuhla.
Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.
9 Ngoba iNkosi ixotshile elifeni phambi kwenu izizwe ezinkulu lezilamandla; lina-ke kakulamuntu ome phambi kwenu kuze kube lamuhla.
“Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu.
10 Umuntu oyedwa kini uzaxotsha inkulungwane, ngoba iNkosi uNkulunkulu wenu yiyo elilwelayo, njengalokho ikhulumile kini.
Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera.
11 Ngakho ziqaphelisiseni ukuthanda iNkosi uNkulunkulu wenu.
Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.
12 Ngoba uba libuyela lokubuyela, linamathele kunsali yalezizizwe, lezi ezisele lani, lithathane lazo, lingene kuzo, lazo kini,
“Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo,
13 yazini lokwazi ukuthi iNkosi uNkulunkulu wenu kayiyikuqhubeka ngokuzixotsha elifeni lezizizwe phambi kwenu; kodwa zizakuba yisifu lomjibila kini, zibe luswazi enhlangothini zenu, lameva emehlweni enu, lize libhubhe liphele kulelilizwe elihle, iNkosi uNkulunkulu wenu elinike lona.
pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
14 Khangelani-ke, ngihamba lamuhla ngendlela yomhlaba wonke. Njalo liyazi enhliziyweni yenu yonke lemphefumulweni wenu wonke ukuthi akukho lelizwi elilodwa elehlulekayo kuwo wonke amazwi amahle iNkosi uNkulunkulu wenu ewakhulumileyo phezu kwenu; wonke ezile kini, akukho lelizwi elilodwa elehlulekayo kuwo.
“Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe.
15 Kuzakuthi-ke, njengalokhu zonke izinto ezinhle iNkosi uNkulunkulu wenu eyazikhuluma kini sezilehlele, ngokunjalo iNkosi izalehlisela zonke izinto ezimbi, ize ilibhubhise liphele kulelilizwe elihle iNkosi uNkulunkulu wenu elinike lona.
Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani.
16 Uba liseqa isivumelwano seNkosi uNkulunkulu wenu eyalilaya sona, lisuke liyekhonza abanye onkulunkulu, likhothame kibo, khona ulaka lweNkosi luzalivuthela, libhubhe masinyane liphele kulelilizwe elihle elinike lona.
Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”

< UJoshuwa 23 >