< UJona 2 >

1 UJona wasekhuleka eNkosini uNkulunkulu wakhe esemathunjini enhlanzi,
Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
2 wathi: Ekuhluphekeni kwami ngakhala eNkosini, yangiphendula; ngisesiswini sengcwaba ngamemeza, wena walizwa ilizwi lami. (Sheol h7585)
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
3 Ngoba wangiphosela enzikini, enhliziyweni yezinlwandle, lempophoma zangihanqa; wonke amagagasi akho lamavinqo akho kwedlula phezu kwami.
Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
4 Ngasengisithi mina: Ngixotshiwe phambi kobuso bakho; kanti ngizabuya ngikhangele ngasethempelini lakho elingcwele.
Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
5 Amanzi angihanqile kuze kube semphefumulweni; inziki ingizingelezele; imihlanga yathandela ikhanda lami.
Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
6 Ngehlela ezisekelweni zezintaba; umhlaba, imigoqo yawo yangihanqa laphakade; kanti wenyuse impilo yami emgodini, Nkosi Nkulunkulu wami.
Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
7 Lapho umphefumulo wami uphela amandla phakathi kwami ngakhumbula iNkosi; lomkhuleko wami wafika kuwe, ethempelini lakho elingcwele.
“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
8 Labo abagcina amanga ayize batshiya umusa wabo.
“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
9 Kodwa mina ngizakwenza umhlatshelo kuwe ngelizwi lokubonga, ngikhokhe lokho engikufungileyo; usindiso ngolweNkosi.
Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
10 INkosi yasikhuluma kuyo inhlanzi, yasimhlanza uJona emhlabathini owomileyo.
Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

< UJona 2 >