< UJoweli 2 >

1 Vuthelani uphondo eZiyoni, lihlabe umkhosi entabeni yami engcwele; kabathuthumele bonke abahlali belizwe, ngoba usuku lweNkosi luyeza, ngoba luseduze.
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 Usuku lomnyama lobumnyama, usuku lwamayezi lomnyama onzima, njengemadabukakusa lembese phezu kwezintaba; isizwe esikhulu lesilamandla, kakuzanga kube khona esinjengaso kusukela endulo, futhi kakusayikuba khona emva kwaso kuze kube yiminyaka yezizukulwana lezizukulwana.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Umlilo uyaqeda phambi kwaso, langemva kwaso kuvutha ilangabi. Phambi kwaso ilizwe lifanana lesivande seEdeni, kodwa ngemva kwaso liyinkangala yencithakalo; yebo kakulakuphunyuka kuso.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Isimo saso sinjengesimo samabhiza, lanjengabagadi bamabhiza ngokunjalo bazagijima.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Bazakweqa njengomsindo wezinqola ezingqongeni zezintaba, njengomsindo welangabi lomlilo oqeda izidindi, njengabantu abalamandla abahlelelwe impi.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Phambi kobuso babo abantu bazakuba lobuhlungu; bonke ubuso buzanyukumala.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Bazagijima njengamaqhawe, bakhwele imiduli njengamadoda empi, bahambe ngulowo lalowo ngezindlela zakhe, kabayikuphambuka emikhondweni yabo.
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 Kabasunduzani omunye lomunye; bazahamba ngulowo lalowo ngomgwaqo wakhe omkhulu; lapho bewela phezu kwesikhali, kabayikulimala.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 Bazahaluzela bedabula umuzi, bagijime phezu komduli, bakhwele bangene ezindlini, bangene ngamawindi njengesela.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 Umhlaba uzanyikinyeka phambi kwabo, amazulu athuthumele; ilanga lenyanga kube mnyama, lezinkanyezi zigodle ukukhanya kwazo.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 Njalo iNkosi izakhupha ilizwi layo phambi kwebutho layo, ngoba inkamba yayo inkulu kakhulu; ngoba ilamandla eyenza ilizwi layo; ngoba usuku lweNkosi lukhulu, luyesabeka kakhulu; ngubani-ke ongalumela?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 Ngakho lakhathesi, itsho iNkosi, phendukelani kimi ngenhliziyo yenu yonke, langokuzila ukudla, langokukhala inyembezi, langokulila.
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 Lidabule inhliziyo yenu, hatshi izembatho zenu, liphendukele eNkosini, uNkulunkulu wenu, ngoba ilesisa lesihawu, iphuza ukuthukuthela, njalo inkulu ngomusa, iyazisola ngobubi.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Ngubani owaziyo, ingaphenduka izisole, itshiye isibusiso ngemva kwayo, umnikelo wokudla lomnikelo wokunathwayo eNkosini, uNkulunkulu wenu.
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Vuthelani uphondo eZiyoni, yehlukanisani ukuzila ukudla, libize umhlangano onzulu,
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 libuthanise abantu, lingcwelise ibandla, lihlanganise abadala, libuthanise abantwana, labamunya amabele; umyeni kaphume ekamelweni lakhe, lomakoti ekamelweni lakhe.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Kakuthi abapristi, izikhonzi zeNkosi, bakhale inyembezi phakathi kwekhulusi lelathi, bathi: Yekela abantu bakho, Nkosi; unganikeli ilifa lakho ehlazweni, ukuthi abahedeni bababuse. Bazatsholoni phakathi kwezizwe ukuthi: Ungaphi uNkulunkulu wabo?
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 Khona iNkosi izatshisekela ilizwe layo, ihawukele abantu bayo.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 Yebo iNkosi izaphendula ithi ebantwini bayo: Khangelani, ngizalithumela amabele lewayini elitsha lamafutha, ukuthi lisuthe ngakho; kangisayikulenza inhlamba phakathi kwezizwe.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 Kodwa ngizasusela khatshana lani okuvela enyakatho, ngikuxotshele elizweni elomileyo leliyinkangala, ubuso bakho buqonde ngaselwandle lwempumalanga, lokucina kwakho ngaselwandle olungemuva; njalo kwenyuke ivumba lakho, kwenyuke iphunga lakho elibi, ngoba kwenze izinto ezinkulu.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Ungesabi, lizwe, jabula uthokoze, ngoba iNkosi yenze izinto ezinkulu.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Lingesabi, zinyamazana zeganga, ngoba amadlelo enkangala asehlumile; ngoba isihlahla sithela isithelo saso, umkhiwa levini kunike amandla akho.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 Lani bantwana beZiyoni, thabani lithokoze eNkosini, uNkulunkulu wenu; ngoba ilinikile izulu lensewula ngokulunga, yalinisela izulu, izulu lensewula lezulu lamuva njengakuqala.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 Lamabala okubhulela azagcwala amabele, lezikhamelo zewayini ziphuphume ngewayini elitsha lamafutha.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 Njalo ngizabuyisela kini iminyaka eyadliwa yintothoviyane, yisikhonyane, leqhwagi, lenswabanda, ibutho lami elikhulu engalithumela phakathi kwenu.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Njalo lizakudla lokudla, lisuthe, lidumise ibizo leNkosi, uNkulunkulu wenu, oliphethe ngokumangalisayo. Njalo abantu bami kabayikuyangiswa lanininini.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 Njalo lizakwazi ukuthi ngiphakathi kukaIsrayeli, lokuthi ngiyiNkosi uNkulunkulu wenu, njalo kakho omunye. Njalo abantu bami kabayikuyangiswa lanininini.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 Kuzakuthi emva kwalokho ngithele uMoya wami phezu kwayo yonke inyama; njalo amadodana enu lamadodakazi enu azaprofetha; abadala benu baphuphe amaphupho, amajaha enu abone imibono.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Yebo, laphezu kwenceku laphezu kwencekukazi ngizathela uMoya wami ngalezonsuku.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 Njalo ngizaveza izimangaliso emazulwini lemhlabeni, igazi, lomlilo, lezinsika zentuthu.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Ilanga lizaphenduka libe ngumnyama, lenyanga ibe ligazi, lungakafiki usuku lweNkosi olukhulu lolwesabekayo.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Kuzakuthi-ke loba ngubani ozabiza ibizo leNkosi asindiswe; ngoba entabeni yeZiyoni leJerusalema kuzakuba khona ukukhululwa, njengokutsho kweNkosi, laphakathi kwabaseleyo iNkosi ezababiza.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< UJoweli 2 >