< UJobe 41 >

1 Ungamhudula yini uLeviyathani ngengwegwe, kumbe ulimi lwakhe ngentambo oyenza itshone?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Ungafaka yini umhlanga ekhaleni lakhe, kumbe ubhoboze umhlathi wakhe ngameva?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Uzakuncenga kanengi yini? Uzakhuluma lawe ngathambileyo yini?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Uzakwenza isivumelwano lawe yini? Uzamthatha abe yinceku kokuphela yini?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Uzadlala laye yini njengenyoni? Kumbe uzambophela amantombazana akho yini?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Abathengi bazathengiselana ngaye yini? Bazakwehlukaniselana ngaye yini phakathi kwabathengisayo?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Uzagcwalisa yini isikhumba sakhe ngezinhlendla, lekhanda lakhe ngemikhonto yenhlanzi?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Beka isandla sakho phezu kwakhe, khumbula impi, ungakwenzi futhi.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Khangela, ithemba lakhe lizakuba ngamanga. Laye uzaphoselwa phansi yini ngokumbona?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Kakho olesihluku sokuthi amvuse. Ngubani-ke yena ongazimisa phambi kwami?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Ngubani onganduleleyo ukuthi ngimbhadale? Okungaphansi kwamazulu wonke ngokwami.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Kangiyikuthula mayelana lezitho zakhe, lendaba yamandla akhe, lobuhle besimo sakhe.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Ngubani ongabonakalisa ubuso besembatho sakhe? Ngubani ongeza lamatomu akhe aphindwe kabili?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Ngubani ongavula iminyango yobuso bakhe? Amazinyo akhe ayesabeka inhlangothi zonke.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Imizila yamahawu akhe ilokuziqhenya, ivalelwe ngophawu oluqinisiweyo.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Elinye lisondele kwelinye, ukuze kungangeni umoya phakathi kwawo.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Ahlangene, abambana, ukuze angehlukaniswa.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Ukuthimula kwakhe kuphazima ukukhanya, lamehlo akhe anjengenkophe zemadabukakusa.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Emlonyeni wakhe kuphuma izihlanti, ziqhatshe ziphume inhlansi zomlilo.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Emakhaleni akhe kuphuma intuthu, njengembiza ebilayo lemihlanga.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Umoya wakhe uvuthela amalahle, lelangabi liphume emlonyeni wakhe.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 Entanyeni yakhe kuhlala amandla, laphambi kwakhe kugiya usizi.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Amavinqo enyama yakhe anamathelene, aqinile kuye, kawanyikinyeki.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Inhliziyo yakhe iqinile njengelitshe, yebo, ilukhuni njengelitshe lokuchola elingaphansi.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Ekuvukeni kwakhe amaqhawe ayesaba, ngenxa yokwephulwa bayazihlambulula.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Ofinyelela kuye ngenkemba angeme, umkhonto, umtshoko, lomdikadika.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Uthatha insimbi njengotshani, ithusi njengogodo olubolileyo.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Umtshoko kawumenzi abaleke; amatshe esavutha aphendulwa nguye abe yizibi.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Isagila sitshaywa njengezibi; uhleka ukugenqeza komdikadika.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Ngaphansi kwakhe kulendengezi ezibukhali; wendlala izinto ezibukhali odakeni.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Wenza inziki zibile njengembiza, enze ulwandle lube njengembiza yamafutha.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Ngemva kwakhe wenza indlela ikhanye; inziki zingathiwa ziyimpunga.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Kakukho emhlabeni okufanana laye, owenziwa angabi lokwesaba.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Ukhangela konke okuphakemeyo; uyinkosi phezu kwabo bonke abantwana bokuzigqaja.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< UJobe 41 >