< UJobe 3 >
1 Emva kwalokho uJobe wavula umlomo wakhe, waqalekisa usuku lwakhe.
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 UJobe wasephendula wathi:
Ndipo Yobu anati:
3 Kalubhubhe usuku engazalwa ngalo, lobusuku okwathiwa ngalo: Kukhulelwe umntwana wesilisa.
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Lolosuku kalube ngumnyama, uNkulunkulu angalunanzi ephezulu, lokukhanya kungalukhanyisi.
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Umnyama lethunzi lokufa kakuluhlenge, iyezi lihlale phezu kwalo, umnyama welanga ulwesabise.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 Lobobusuku, umnyama ububambe, lungathokozi ensukwini zomnyaka, lungezi kunani lezinyanga.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 Khangela, lobobusuku kabube yinyumba, umsindo wentokozo ungangeni kubo.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 Kababuqalekise abaqalekisi bosuku, abalungele ukuvusa uLeviyathani.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Zibe mnyama inkanyezi zokusa kwabo, bulindele ukukhanya, kodwa kungabi khona, bungaboni inkophe zokusa.
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Ngoba bungavalanga iminyango yesisu sikamama wami, bungafihlanga usizi emehlweni ami.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Kungani ngingafanga kusukela esizalweni, ngiphele ekuphumeni kwami esiswini?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Kungani amadolo angandulela? Kungani lamabele ukuthi ngimunye?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 Ngoba khathesi ngabe ngacambalala ngathula, ngalala, khona ngaba lokuphumula,
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 kanye lamakhosi labeluleki bomhlaba abazakhela amanxiwa,
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 kumbe kanye leziphathamandla ezazilegolide ezagcwalisa izindlu zazo ngesiliva.
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Kumbe njengomphunzo ofihliweyo ngingabi khona, njengensane ezingabonanga ukukhanya.
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 Lapho ababi bayekela ukuhlupha, lapho abakhathele ngamandla bephumula.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 Izibotshwa ziyaphumula ndawonye, kazizwa ilizwi lomcindezeli.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 Omncinyane lomkhulu balapho, lesigqili sikhululekile enkosini yaso.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Kungani enika ukukhanya kohluphekayo, lempilo kwabalokubaba komphefumulo;
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 abalindele ukufa, kodwa kungekho, bekugebha kulenotho efihliweyo,
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 abathabayo kakhulu ngentokozo, bajabule lapho bethola ingcwaba?
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Emuntwini yini, ondlela yakhe ifihliwe, uNkulunkulu ambiyeleyo?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 Ngoba ukububula kwami kuza phambi kokudla kwami, lokubhonga kwami kuthululeka njengamanzi.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Ngoba engikwesabayo ngokwesaba sekungehlele, lengilovalo ngakho kufikile kimi.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 Ngangingahlalisekanga, ngingaphumuli, ngingelakuthula, lohlupho lweza.
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”