< UJobe 19 >
1 Wasephendula uJobe wathi:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Koze kube nini lihlupha umphefumulo wami, lingiphahlaza ngamazwi?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 Lezizikhathi ezilitshumi lingithela ngehlazo; kalilanhloni, lingiphatha kubi.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 Uba-ke kuliqiniso ukuthi ngiduhile, ukuduha kwami kuzahlala lami.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Uba isibili lizikhukhumeza phezu kwami, liphikisane lami ngehlazo lami,
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 yazini-ke ukuthi nguNkulunkulu ongihlanekeleyo, wangigombolozela ngembule lakhe.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Khangela, ngiyamemeza ngithi: Okubi! Kodwa kangiphendulwa. Ngicela usizo, kodwa akulasahlulelo.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Uyivalile indlela yami ngomduli ukuze ngingedluli, wamisa umnyama emikhondweni yami.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Ungihlubule udumo lwami, wasusa umqhele wekhanda lami.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Ungibhidlizile inhlangothi zonke, sengihambile, ulisiphule ithemba lami njengesihlahla.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 Ulumathisile ulaka lwakhe kimi, ungibale njengezitha zakhe kuye.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Amabutho akhe afika kanyekanye, abuthelela indlela yawo emelene lami, amisa inkamba agombolozela ithente lami.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Ubeke abafowethu khatshana lami, labangaziyo isibili sebengabemzini kimi.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Izihlobo zami zinyamalele, labazana lami bangikhohliwe.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Abahlala endlini yami lencekukazi zami bangibala njengowezizwe; ngingumfokazi emehlweni abo.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 Ngabiza inceku yami, kodwa kayiphendulanga; ngayincenga ngomlomo wami.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Umoya wami uyenyanyeka kumkami, sengiyisinengiso kumadodana esizalo sami.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Labantwana abancinyane bayangidelela; ngasukuma, basebekhuluma bemelene lami.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 Bonke abantu besifuba sami banengwa yimi, labo ebengibathanda sebengiphendukele.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Ithambo lami linamathelana lesikhumba sami lenyama yami, njalo ngiphephe ngesikhumba samazinyo ami.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Ngihawukelani, ngihawukelani, lina bangane bami; ngoba isandla sikaNkulunkulu singithintile.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Lingizingelelani njengoNkulunkulu, lingeneliswa yinyama yami?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Kungathi ngabe khathesi amazwi ami abhaliwe! Kungathi ngabe acindezelwe egwalweni!
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 Ngabe abazwe ngepheni yensimbi langomnuso edwaleni kuze kube nininini!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Ngoba mina ngiyazi ukuthi umhlengi wami uyaphila, lekupheleni uzakuma emhlabathini.
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 Lapho sekutshabalalise lokhu emva kwesikhumba sami, kanti enyameni yami ngizambona uNkulunkulu,
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 mina engizazibonela yena, lamehlo ami azabona, hatshi omunye. Izinso zami seziphelile ngaphakathi kwami.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Kodwa lithi: Kungani simzingela? Ngoba impande yendaba itholakala kimi.
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Lina yesabeni inkemba, ngoba ulaka luletha izijeziso zenkemba, ukuze lazi ukuthi sikhona isahlulelo.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”