< UJobe 13 >
1 Khangela, konke ilihlo lami likubonile, indlebe yami izwile yakuqedisisa.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Njengokolwazi lwenu lami ngiyakwazi; kangiphansi kulani.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 Kodwa mina ngizakhuluma loSomandla, ngifisa ukuqondisana loNkulunkulu.
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 Kodwa lina-ke ligcona ngamanga, lonke lingabelaphi abangelamsebenzi.
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 Kungathi ngabe liyathula lithi zwi; lokhu kube yinhlakanipho kini!
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Ake lizwe ukuzivikela kwami, lilalele impikiso zendebe zami.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Lizamkhulumela uNkulunkulu ngokubi, limkhulumele ngenkohliso yini?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Lizakwemukela ubuso bakhe, lizammela yini uNkulunkulu?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Kuzakuba kuhle yini lapho elihlola? Lizamkhohlisa yini njengokhohlisa umuntu?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Isibili uzalisola, uba lisemukela ubuso ensitha.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Ubukhulu bakhe kabulethusi yini, lokwesabeka kwakhe kulehlele?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Izikhumbuzo zenu ziyizaga zomlotha, izivikelo zenu ziyizivikelo zebumba.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Thulani lingiyekele, ukuze ngikhulume mina; kungehlele loba kuyini.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Ngizayithathelani inyama yami ngamazinyo ami, ngibeke impilo yami esandleni sami?
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Lanxa ezangibulala, ngizathemba kuye. Kanti ngizazimela indlela zami phambi kwakhe.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 Njalo uzakuba lusindiso lwami; ngoba umzenzisi kayikuza phambi kwakhe.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Zwisisani ilizwi lami, lengcazelo yami ngendlebe zenu.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Khangelani-ke, sengilubeke kuhle udaba lwami, ngiyazi ukuthi mina ngizalungisiswa.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Ngubani lowo ozaphikisana lami? Nxa khathesi ngithula ngizaphela.
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 Kuphela ungenzi izinto ezimbili kimi; khona ngingayikucatshela ubuso bakho.
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Susela khatshana lami isandla sakho, lokwesabeka kwakho kungangethusi.
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Ubusungibiza, mina ngizaphendula; kumbe ngikhulume, ungiphendule.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Zingaki iziphambeko lezono engilazo? Ngazisa isiphambeko sami lesono sami.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Ufihlelani ubuso bakho, ungiphathe njengesitha sakho?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Uzakwethusa yini ihlamvu eliphephethekayo? Njalo uzaxotshana lomule owomileyo yini?
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 Ngoba ubale izinto ezibabayo umelene lami, wangenza ngadla ilifa leziphambeko zobutsha bami.
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 Ufake lenyawo zami esigodweni, waqaphela zonke indlela zami, wazidweba uluphawu empandeni zezinyawo zami.
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 Yena-ke njengokubolileyo uyaguga, njengesembatho inundu esidlayo.
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.