< UJobe 12 >

1 Wasephendula uJobe wathi:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Ngoba isibili lingabantu, lenhlakanipho izakufa lani.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Lami ngilengqondo njengani, kangiphansi kulani. Njalo ngubani ongelazo izinto ezinje?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Ngiyinhlekisa kumngane wami, obiza kuNkulunkulu amphendule; olungileyo oqondileyo uyinhlekisa.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Uyisibane esidelelekayo emnakanweni wowonwabileyo; ulungele ukutshelela ngonyawo.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Amathente abaphangi alokuthula, labamthukuthelisayo uNkulunkulu bavikelekile, kulowo oletha uNkulunkulu esandleni sakhe.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Kodwa-ke buza khathesi inyamazana, zizakufundisa, lenyoni zamazulu, zizakutshela.
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Kumbe khuluma lomhlaba, uzakufundisa, lenhlanzi zolwandle zizakulandisela.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Ngubani ongaziyo phakathi kwakho konke lokhu ukuthi isandla sikaJehova sikwenzile lokhu?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 Okusesandleni sakhe umphefumulo wakho konke okuphilayo, lomoya wayo yonke inyama yomuntu.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Indlebe kayihloli yini amazwi, njengolwanga luzinambithela ukudla?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Kwabadala kakhulu kulenhlakanipho, lebudeni bezinsuku kulokuqedisisa.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 Kuye kukhona inhlakanipho lamandla, uleseluleko lokuqedisisa.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Khangela, udiliza, kungabe kusakhiwa; uvalela umuntu, kungabe kusavulwa.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Khangela, uvimbela amanzi, atshe; abesewathuma, agenqule umhlaba.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Kuye kukhona amandla lenhlakanipho; okhohlisiweyo lomkhohlisi bangabakhe.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Ukhupha abeluleki bahambe behlutshulwe, enze abehluleli babe yizithutha.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Uthukulula isibopho samakhosi, abophe umbhinco enkalweni zawo.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Ukhupha abapristi bahambe behlutshulwe, awise abalamandla.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Uphambula inkulumo yabathembekileyo, asuse ukuqedisisa kwabasebekhulile.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Uthela ukudelela phezu kweziphathamandla, axegise umbhinco wabalamandla.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Wembula izinto ezijulileyo ezisemnyameni, akhuphele ekukhanyeni ithunzi lokufa.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Enze izizwe zibe zinkulu, abesezichitha; andise izizwe, abesezisusa.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Ususa inhliziyo yenhloko zabantu bomhlaba, aziduhise enkangala engelandlela.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 Ziphumputhe emnyameni kungelakukhanya, uzenza zidiyazele njengodakiweyo.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< UJobe 12 >