< UJeremiya 7 >

1 Ilizwi elafika kuJeremiya livela eNkosini lisithi:
Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
2 Mana esangweni lendlu yeNkosi umemezele khona lelilizwi uthi: Zwanini ilizwi leNkosi, lina bonke bakoJuda, abangena kulamasango ukuzakhonza iNkosi.
“Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
3 Itsho njalo INkosi yamabandla, uNkulunkulu wakoIsrayeli: Lungisani indlela zenu lezenzo zenu, khona ngizalenza ukuthi lihlale kulindawo.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
4 Lingathembi lina emazwini amanga okuthi: La alithempeli leNkosi, ithempeli leNkosi, ithempeli leNkosi.
Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
5 Ngoba uba lilungisisa lokulungisa izindlela zenu lezenzo zenu; uba lisenza lokwenza isahlulelo phakathi komuntu lomakhelwane wakhe;
Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
6 lingacindezeli owezizweni, intandane, lomfelokazi, lingachithi igazi elingelacala kulindawo; futhi lingalandeli abanye onkulunkulu ukuze kube kubi kini;
ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
7 khona ngizalenza ukuthi lihlale kulindawo, elizweni engalinika oyihlo, kusukela endulo kuze kube nininini.
Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
8 Khangelani, lina lithembela emazwini amanga angasizi lutho.
Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
9 Lizakweba, libulale, lifebe, lifunge amanga, litshisele uBhali impepha, lilandele abanye onkulunkulu elingabaziyo yini?
“Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
10 Beselisiza lime phambi kwami kulindlu, ebizwa ngebizo lami, lithi: Sikhululwe ukuze senze zonke lezizinengiso.
ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
11 Indlu le, ebizwa ngebizo lami, isibe lubhalu lwabaphangi emehlweni enu yini? Khangelani, mina sengibonile, itsho iNkosi.
Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
12 Ngoba yanini khathesi endaweni yami eseShilo, lapho engamisa khona ibizo lami kuqala, libone engikwenzileyo kiyo ngenxa yobubi babantu bami uIsrayeli.
“‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
13 Khathesi-ke, ngoba lenzile yonke le imisebenzi, itsho iNkosi, njalo ngikhulumile lani, ngivuka ngovivi ngikhuluma, kodwa kalizwanga, ngalibiza, kodwa kaliphendulanga;
Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
14 ngakho ngizakwenza kulindlu, ebizwa ngebizo lami, elithemba kiyo, lakundawo engayinika lina laboyihlo, njengalokho engakwenza eShilo.
choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
15 Njalo ngizalixotsha lisuke ebusweni bami, njengalokho ngaxotsha bonke abafowenu, inzalo yonke kaEfrayimi.
Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
16 Ngakho wena ungabakhulekeli lababantu, ungabaphakamiseli ukukhala loba umkhuleko, ungalabheli kimi, ngoba kangiyikukuzwa.
“Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
17 Kawukuboni yini abakwenza emizini yakoJuda lezitaladeni zeJerusalema?
Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
18 Abantwana batheza inkuni, laboyise baphembe umlilo, labesifazana baxove inhlama, ukuze benzele indlovukazi yamazulu amaqebelengwana, bathululele abanye onkulunkulu iminikelo yokunathwayo, ukuze bangithukuthelise.
Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
19 Bathukuthelisa mina yini? itsho iNkosi. Kabazenzeni yini kuze kusanganiseke ubuso babo?
Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
20 Ngakho itsho njalo iNkosi uJehova: Khangela, intukuthelo yami lolaka lwami kuzathululelwa kulindawo, phezu komuntu, laphezu kwenyamazana, laphezu kwezihlahla zasendle, laphezu kwesithelo somhlabathi; njalo kuzakutsha, kungacitshwa.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
21 Itsho njalo INkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Fakani iminikelo yenu yokutshiswa kanye lemihlatshelo yenu, lidle inyama.
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
22 Ngoba kangikhulumanga kuboyihlo, njalo kangibalayanga ngosuku engabakhupha ngalo elizweni leGibhithe, mayelana lendaba zeminikelo yokutshiswa kumbe imihlatshelo.
Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
23 Kodwa ngabalaya le into ngisithi: Lalelani ilizwi lami, njalo ngizakuba nguNkulunkulu wenu, lina-ke libe ngabantu bami; njalo hambani ngayo yonke indlela engililaya yona, ukuze kulilungele.
koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
24 Kodwa kabalalelanga, kabathobanga indlebe yabo; kodwa bahamba ngamacebo, ngenkani yenhliziyo yabo embi, bahlehlela nyovane, hatshi-ke phambili.
Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
25 Kusukela osukwini oyihlo abaphuma ngalo elizweni leGibhithe kuze kube yilolusuku, ngithume kini zonke inceku zami, abaprofethi, insuku ngensuku ngivuka ngovivi, ngithuma.
Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
26 Kanti kabangilalelanga, njalo kababekanga indlebe yabo, kodwa benza intamo yabo yaba lukhuni; benza kubi kulaboyise.
Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
27 Ngakho uzakhuluma wonke lamazwi kibo, kodwa kabayikukulalela; futhi uzababiza, kodwa kabayikukuphendula.
“Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
28 Ngakho uzakuthi kibo: Lesi yisizwe esingalaleli ilizwi leNkosi, uNkulunkulu waso, lesingemukeli ukulaywa; iqiniso liphelile, liqunyiwe emlonyeni waso.
Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
29 Gela inwele zakho, wena Jerusalema, uzilahle, uphakamise isililo emadundulwini; ngoba iNkosi isalile yasidela isizukulwana solaka lwayo.
“Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
30 Ngoba abantwana bakoJuda benzile ububi emehlweni ami, itsho iNkosi; babekile izinengiso zabo endlini ebizwa ngebizo lami, ukuze bayingcolise.
“Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
31 Bakhile-ke indawo eziphakemeyo zeTofethi, ezisesihotsheni sendodana kaHinomu, ukuze batshise amadodana abo lamadodakazi abo ngomlilo; engingabalayanga khona, lokungavelanga enhliziyweni yami.
Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
32 Ngakho khangela, insuku ziyeza, itsho iNkosi, lapho engasayikubizwa ngokuthi yiTofethi, loba isihotsha sendodana kaHinomu, kodwa isihotsha sokubulala; ngoba bazangcwaba eTofethi, kuze kungabi landawo.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
33 Lezidumbu zalababantu zizakuba yikudla kwenyoni zamazulu, lezezinyamazana zomhlaba, kungekho ozazethusa.
Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
34 Khona ngizakwenza kuphele emizini yakoJuda lezitaladeni zeJerusalema ilizwi lenjabulo, lelizwi lentokozo, ilizwi lomyeni, lelizwi likamakoti, ngoba ilizwe lizakuba lunxiwa.
Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”

< UJeremiya 7 >