< UJeremiya 5 >

1 Hambani liye le lale ezitaladeni zeJerusalema, libone khathesi, lazi, lidinge ezindaweni zayo ezingamagceke, uba lingathola umuntu, uba ekhona owenza isahlulelo, odinga iqiniso; khona ngizayithethelela.
“Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu, mudzionere nokha, funafunani mʼmabwalo ake. Ngati mungapeze munthu mmodzi amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi, ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.
2 Loba-ke besithi: Kuphila kukaJehova; kanti bafunga amanga.
Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ komabe akungolumbira mwachinyengo.”
3 Nkosi, amehlo akho kawakho eqinisweni yini? Ubatshayile, kodwa kabezwanga buhlungu; ubaqothule, kodwa bala ukwemukela ukulaywa. Benzile ubuso babo bube lukhuni kuledwala, bala ukuphenduka.
Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona? Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka; munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro. Anawumitsa mitima yawo ngati mwala ndipo anakaniratu kulapa.
4 Mina ngasengisithi: Qiniso, laba ngabayanga, bayizithutha; ngoba kabayazi indlela yeNkosi, isahlulelo sikaNkulunkulu wabo.
Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe; anthu ochita zopusa. Sadziwa njira ya Yehova, sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.
5 Mina ngizakuya kwabakhulu, ngikhulume labo, ngoba bona bayayazi indlela yeNkosi, isahlulelo sikaNkulunkulu wabo; kodwa labo kanyekanye balephulile ijogwe, baqamula izibopho.
Tsono ndidzapita kwa atsogoleri ndi kukayankhula nawo; ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova, amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.” Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova ndipo anadula msinga zawo.
6 Ngakho-ke isilwane esiphuma ehlathini sizababulala, impisi yezinkangala ibachithe, ingwe ilinde imelene lemizi yabo; wonke ophuma kiyo uzadatshudatshulwa; ngoba iziphambeko zabo zinengi, ukuhlehlela nyovane kwabo kwandile.
Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha, mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga, kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.
7 Ngingakuthethelela njani ngalokhu? Abantwana bakho bangidelile, bafunga ngabangeyisibo onkulunkulu. Sengibasuthisile, basebefeba, babuthana ngamaxuku endlini yezifebe.
Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita? Ana anu andisiya Ine ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse. Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa, komabe iwo anachita chigololo namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.
8 Babenjengamabhiza asuthayo ekuseni, bakhonya, omunye lomunye kumfazi kamakhelwane wakhe.
Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa, aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.
9 Kangiyikujezisa yini ngenxa yalezizinto? itsho iNkosi; kumbe umphefumulo wami kawuyikuphindisela yini esizweni esinjengalesi?
Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi nʼkuleka kuwulipsira mtundu woterewu?
10 Yenyukelani emidulwini yayo, lichithe, kodwa lingenzi isiphetho esipheleleyo; susani ingatsha zayo, ngoba kazisizo zeNkosi.
“Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga, koma musakayiwononge kotheratu. Sadzani nthambi zake pakuti anthu amenewa si a Yehova.
11 Ngoba indlu kaIsrayeli lendlu kaJuda zenze ngenkohliso enkulu zimelene lami, itsho iNkosi.
Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”
12 Bayiphikile iNkosi, bathi: Kayisiyo; njalo ububi kabuyikusehlela, futhi kasiyikubona inkemba loba indlala.
Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti, “Yehova sangachite zimenezi! Choyipa sichidzatigwera; sitidzaona nkhondo kapena njala.
13 Labaprofethi bazakuba ngumoya, lelizwi kalikho kubo; kuzakwenziwa njalo kibo!
Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo; ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova. Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”
14 Ngalokho itsho njalo iNkosi uNkulunkulu wamabandla: Ngoba likhuluma lelilizwi, khangela, ngizakwenza amazwi ami emlonyeni wakho abe ngumlilo, lalababantu babe zinkuni, njalo uzabaqothula.
Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti, “Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa, tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.
15 Khangelani, ngizaletha phezu kwenu isizwe esivela khatshana, ndlu kaIsrayeli, itsho iNkosi; yisizwe esilamandla, yisizwe esidala, isizwe ongalwaziyo ulimi lwaso, longayikuzwa esikukhulumayo.
Inu Aisraeli,” Yehova akuti, “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali, ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo, mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa, zimene akunena inu simungazimvetse.
16 Isamba saso semitshoko sinjengengcwaba elivulekileyo; bonke bangamaqhawe.
Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri; onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.
17 Njalo sizakudla isivuno sakho lokudla kwakho; sizakudla amadodana akho lamadodakazi akho; sizakudla izimvu zakho lenkomo zakho; sizakudla ivini lakho lomkhiwa wakho; lemizi yakho ebiyelweyo othembela kiyo, sizayithelela ubuyanga ngenkemba.
Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu, adzapha ana anu aamuna ndi aakazi; adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu, adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu. Ndi malupanga awo adzagwetsa mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.
18 Kodwa langalezonsuku, itsho iNkosi, kangiyikwenza isiphetho esipheleleyo kini.
“Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova.
19 Kuzakuthi-ke lapho lisithi: INkosi uNkulunkulu wethu yenzeleni zonke lezizinto kithi? Khona uzakutsho kubo uthi: Njengoba lingidelile, lakhonza onkulunkulu bemzini elizweni lakini, ngokunjalo lizakhonza abezizwe elizweni elingeyisilo lenu.
Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”
20 Memezelani lokhu endlini kaJakobe, likuzwakalise koJuda, lisithi:
“Lengeza izi kwa ana a Yakobo ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,
21 Zwanini-ke lokhu, lina bantu abayizithutha labangelangqondo, elilamehlo, kodwa lingaboni, elilendlebe, kodwa lingezwa.
Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru, inu amene maso muli nawo koma simupenya, amene makutu muli nawo koma simumva.
22 Kalingesabi yini? itsho iNkosi; kaliyikuthuthumela phambi kwami yini, engabeka itshebetshebe laba ngumngcele wolwandle ngesimiso saphakade olungeledlule? Lanxa amagagasi alo etshayana kube kanti angenqobe; lanxa ehlokoma kube kanti kawayikudlula phezu kwawo.
Kodi simuyenera kuchita nane mantha?” Akutero Yehova. “Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga? Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja, malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo. Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo; mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.
23 Kodwa lababantu balenhliziyo evukelayo lephikayo; baphambukile, bahamba.
Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.
24 Futhi kabatsho enhliziyweni zabo ukuthi: Ake sesabe iNkosi uNkulunkulu wethu, enika izulu lakuqala lelamuva ngesikhathi salo, esigcinela amaviki amisiweyo esivuno.
Sananenepo mʼmitima mwawo kuti, ‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu. Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika. Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’
25 Iziphambeko zenu ziphambule lezizinto, lezono zenu zaligodlela okuhle.
Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi; ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.
26 Ngoba phakathi kwabantu bami kutholakala abakhohlakeleyo; bacatheme njengabathiya inyoni; babeka umgibe ochithayo, babambe abantu.
“Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.
27 Njengezongo ligcwele inyoni, zinjalo izindlu zabo zigcwele inkohliso; ngakho-ke sebebakhulu, banothile.
Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo ngati zikwere zodzaza ndi mbalame. Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.
28 Bazimukile, bancwaba, yebo, bedlula imisebenzi yomubi; kabameli udaba, udaba lwezintandane, kube kanti bayaphumelela; lelungelo labaswelayo kabalahluleli.
Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala. Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire; saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino, sateteza ufulu wa anthu osauka.
29 Kangiyikubajezisa ngalezizinto yini? kutsho iNkosi. Umphefumulo wami kawuyikuphindisela esizweni esinjengalesi yini?
Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi? Kodi ndisawulipsire mtundu woterewu? Akutero Yehova.
30 Okwethusayo lokwesabekayo kwenzakele elizweni.
“Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri chachitika mʼdzikomo:
31 Abaprofethi baprofetha ngamanga, labapristi babusa ngezandla zabo; labantu bami bakuthanda kunjalo; kodwa lizakwenzani ekupheleni kwakho?
Aneneri akunenera zabodza, ndipo ansembe akuvomerezana nawo, ndipo anthu anga akukonda zimenezi. Koma mudzatani potsiriza?

< UJeremiya 5 >