< UJeremiya 49 >
1 Mayelana labantwana bakoAmoni itsho njalo iNkosi: UIsrayeli kalamadodana yini? Kalayo indlalifa yini? Kungani uMilkomu esidla ilifa lakoGadi, labantu bakhe behlala emizini yayo?
Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
2 Ngakho khangela, insuku ziyeza, itsho iNkosi, lapho ngizakwenza ukuthi kuzwakale umkhosi wempi eRaba yabantwana bakoAmoni; njalo izakuba yinqumbi yencithakalo, lamadodakazi ayo atshiswe ngomlilo; loIsrayeli adle ilifa labadla ilifa lakhe, itsho iNkosi.
Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
3 Qhinqa isililo, Heshiboni, ngoba iAyi ichithiwe; khalani, madodakazi eRaba, libhince amasaka, lilile, liye le lale ezintangweni; ngoba uMilkomu uzahamba ekuthunjweni, abapristi bakhe leziphathamandla zakhe ndawonye.
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
4 Uzincomelani ngezihotsha? Isihotsha sakho siyageleza, ndodakazi ehlehlela nyovane, ethemba amagugu ayo, usithi: Ngubani ozakuza kimi?
Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
5 Khangela, ngizakwehlisela phezu kwakho uvalo, itsho iNkosi, uJehova wamabandla, luvela kubo bonke abakuhanqileyo; njalo lizaxotshwa, ngulowo lalowo phambi kwakhe; njalo kakho ozabutha ozulayo.
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
6 Kodwa emva kwalokho ngizabuyisa ukuthunjwa kwabantwana bakoAmoni, itsho iNkosi.
“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
7 Mayelana leEdoma, itsho njalo iNkosi yamabandla: Kakuselanhlakanipho yini eThemani? Icebo liphelile yini kwabaqedisisayo? Inhlakanipho yabo isinyamalele yini?
Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
8 Balekani, buyelani emuva, hlalani endaweni ejulileyo, bahlali beDedani; ngoba ngizakwehlisela inhlupheko kaEsawu phezu kwakhe, isikhathi sokumhambela kwami.
Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
9 Uba abavuni bamavini befika kuwe bebengayikutshiya yini umkhothozo? Uba amasela efika ebusuku, azaphanga aze anele?
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Kodwa mina ngimhlubule uEsawu, ngizembule indawo zakhe zensitha, ukuze angabi lakho ukucatsha; inzalo yakhe ichithiwe, labafowabo, labomakhelwane bakhe, yena kasekho.
Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
11 Tshiya izintandane zakho, mina ngizazilondoloza ziphila, labafelokazi bakho kabathembele kimi.
‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
12 Ngoba itsho njalo iNkosi: Khangela, labo okugwetshwa kwabo kwakungeyisikho ukunatha inkezo bazayinatha lokuyinatha, wena-ke nguwe yini ozayekelwa ungajeziswanga ngokupheleleyo? Kawuyikuyekelwa ungelacala, kodwa isibili uzanatha.
Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
13 Ngoba ngifungile ngami uqobo, itsho iNkosi, ukuthi iBhozira izakuba ngokwesabekayo, ibe lihlazo, ibe lunxiwa, ibe yisiqalekiso; lemizi yayo yonke izakuba ngamanxiwa aphakade.
Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
14 Ngizwile umbiko ovela eNkosini, lesithunywa sithunywe phakathi kwezizwe, sisithi: Buthanani, lize limelane layo, lisukumele impi.
Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
15 Ngoba khangela, ngizakwenza ube mncinyane phakathi kwezizwe, udeleleke phakathi kwabantu.
“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Ukwesabeka kwakho kukukhohlisile, ukuziqhenya kwenhliziyo yakho, wena ohlala ezingoxweni zamadwala, obamba izingqonga zoqaqa. Loba usenza isidleke sakho sibe phezulu njengokhozi, ngizakwehlisa usuka khona, itsho iNkosi.
Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
17 IEdoma layo izakuba yinto eyesabekayo; wonke odlula kuyo uzamangala kakhulu, ancife ngenxa yenhlupheko yonke yayo.
“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Njengokuchithwa kweSodoma leGomora, labomakhelwane bayo, itsho iNkosi; kakulamuntu ozahlala khona, kakulandodana yomuntu ezahlala khona njengowezizwe.
Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
19 Khangela, njengesilwane esivela ekukhukhumaleni kweJordani uzakwenyuka emelene lendawo yokuhlala okungapheliyo, kodwa ngizahle ngimgijimise asuke kuyo; njalo ngubani okhethiweyo engingammisa emelene layo? Ngoba ngubani onjengami? Ngubani-ke ozangibizela ukulandisa? Njalo nguwuphi lowomelusi ongema phambi kwami?
“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Ngakho, zwanini icebo leNkosi elicebe imelene leEdoma, lemicabango yayo eyicabange emelene labahlali beThemani: Isibili abancinyane bomhlambi bazabadonsa; isibili izachitha indawo yabo yokuhlala phezu kwabo.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Ngomsindo wokuwa kwabo umhlaba uyazamazama; ukukhala, umsindo wakho wezwakala eLwandle oluBomvu.
Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Khangela, uzakwenyuka andize ngesiqubu njengokhozi, elulele impiko zakhe phezu kweBhozira; lenhliziyo yamaqhawe eEdoma ngalolosuku izakuba njengenhliziyo yowesifazana ohelelwayo.
Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
23 Mayelana leDamaseko. IHamathi leArpadi kuyangekile, ngoba bazwile umbiko omubi; bancibilika, kulokunqineka elwandle, kungeke kube lokuthula.
Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 IDamaseko isibuthakathaka, itshibilike ukuze ibaleke, lokwethuka kuyibambile, ukucindezelwa losizi kuyibambile njengobelethayo.
Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Kawutshiywanga njani umuzi wodumo, umuzi wentokozo yami!
Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Ngakho amajaha awo azawela ezitaladeni zawo, lawo wonke amadoda empi azabhujiswa ngalolosuku, itsho iNkosi yamabandla.
Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 Ngizaphemba-ke umlilo emdulini weDamaseko, ozaqothula izigodlo zikaBenihadadi.
“Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 Mayelana leKedari njalo mayelana lemibuso yeHazori owayitshayayo uNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni: Itsho njalo iNkosi: Sukumani, lenyukele eKedari, lichithe amadodana empumalanga.
Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Bazathatha amathente abo lemihlambi yabo, amakhetheni abo lempahla yabo yonke lamakamela abo bazazithwalela khona; bamemeze kibo bathi: Uvalo enhlangothini zonke.
Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 Balekani, lizulazule kakhulu, lihlale ngokujula, lina bahlali beHazori, itsho iNkosi; ngoba uNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni waceba icebo emelene lani, wacabanga umcabango emelene lani.
“Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 Sukumani, lenyuke limelene lesizwe esonwabileyo, esihlala ekuvikelekeni, itsho iNkosi, esingelamasango, esingelamigoqo, esizihlalele sodwa.
“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 Lamakamela abo azakuba yimpango, lemihlambi yezifuyo zabo izakuba yimpango; njalo ngizabachithachitha kuyo yonke imimoya, abaphoselwe engonsini, ngilethe inkathazo yabo evela inhlangothi zonke zaso, itsho iNkosi.
Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 LeHazori izakuba yindawo yokuhlala yamakhanka, unxiwa kuze kube nininini; kakuyikuhlala muntu khona, lendodana yomuntu kayiyikuhlala kuyo njengowezizwe.
“Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 Ilizwi leNkosi elafika kuJeremiya umprofethi limelene leElamu ekuqaleni kokubusa kukaZedekhiya, inkosi yakoJuda, lisithi:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 Itsho njalo iNkosi yamabandla: Khangela, ngizakwephula idandili leElamu, induna yamandla abo.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 Ngilethele iElamu imimoya emine evela emikhawulweni emine yamazulu, ngibahlakazele kuyo yonke leyomimoya; njalo kakuyikuba khona isizwe lapho abaxotshiweyo beElamu abangayikufika khona.
Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 Ngoba ngizakwenza abeElamu besabe phambi kwezitha zabo laphambi kwalabo abadinga impilo yabo, ngibehlisele okubi, ukuvutha kolaka lwami, itsho iNkosi, ngithume inkemba emva kwabo, ngize ngibaqede.
A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 Ngizamisa-ke isihlalo sami sobukhosi eElamu, ngichithe kuyo inkosi leziphathamandla, itsho iNkosi.
Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 Kodwa kuzakuthi ekucineni kwezinsuku ngibuyise ukuthunjwa kukaElamu, itsho iNkosi.
“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.