< UJeremiya 44 >

1 Ilizwi elafika kuJeremiya ngawo wonke amaJuda ayehlala elizweni leGibhithe ahlala eMigidoli leThahaphanesi leNofi lelizweni lePatrosi, lisithi:
Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
2 Itsho njalo iNkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Lina likubonile konke okubi engakwehlisela phezu kweJerusalema laphezu kwayo yonke imizi yakoJuda. Khangelani-ke, lamuhla ilunxiwa, njalo kakho ohlala phakathi kwayo,
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
3 ngenxa yobubi babo ababenzileyo, ukungithukuthelisa, ngokuyatshisa impepha, ngokukhonza abanye onkulunkulu abangabaziyo, bona, lina, laboyihlo.
Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
4 Kanti ngathuma kini inceku zami zonke abaprofethi, ngivuke ngovivi ngathuma, ngisithi: Ake lingayenzi linto enengekayo engiyizondayo.
Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
5 Kodwa kabalalelanga kababekanga indlebe yabo, ukuthi baphenduke ebubini babo, ukuze bangatshiseli abanye onkulunkulu impepha.
Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
6 Ngakho kwathululwa intukuthelo yami lolaka lwami, kwavutha emizini yakoJuda lezitaladeni zeJerusalema; zaze zaba lunxiwa lencithakalo, njengalamuhla.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
7 Ngakho-ke, itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu wamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Libenzelani ububi obukhulu kangaka limelene lemiphefumulo yenu, ukuthi liziqumele indoda lomfazi, umntwana losane, basuke phakathi kwakoJuda, ukuze lingazitshiyeli insali,
“Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
8 ngokungithukuthelisa ngemisebenzi yezandla zenu, ngokutshisela abanye onkulunkulu impepha elizweni leGibhithe, lapho eseliyehlala khona njengabezizwe, ukuze liziqume, lokuze libe yisiqalekiso lehlazo phakathi kwazo zonke izizwe zomhlaba?
Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
9 Selakhohlwa yini izinto ezimbi zaboyihlo, lezinto ezimbi zamakhosi akoJuda, lezinto ezimbi zabomkabo, lezinto zenu ezimbi, lezinto ezimbi zabomkenu, abazenza elizweni lakoJuda lezitaladeni zeJerusalema?
Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
10 Kabadabukanga kuze kube lamuhla, kabesabanga, kabahambanga ngomlayo wami langezimiso zami engazibeka phambi kwenu laphambi kwaboyihlo.
Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
11 Ngakho itsho njalo iNkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Khangelani, ngimisa ubuso bami bumelene lani ngokubi ukuze ngiqume uJuda wonke.
“Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
12 Ngithathe insali yakoJuda, abamise ubuso babo ukungena elizweni leGibhithe ukuhlala khona njengabezizwe; njalo bonke bazaphela bawe elizweni leGibhithe; baqedwe ngenkemba langendlala; kusukela komncinyane kuze kube komkhulu bafe ngenkemba langendlala; babe yisifungo, babe ngokwesabisayo, babe yisiqalekiso, babe lihlazo.
Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
13 Ngoba ngizajezisa labo abahlezi elizweni leGibhithe, njengoba ngajezisa iJerusalema, ngenkemba, ngendlala, langomatshayabhuqe wesifo;
Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
14 ukuze insali yakoJuda efikileyo ukuhlala khona njengowezizwe elizweni leGibhithe ingabi lophunyukayo losilayo, ukubuyela elizweni lakoJuda, umphefumulo wayo ofisa ukubuyela kulo ukuhlala khona; ngoba kabayikubuyela, ngaphandle kwabaphunyukileyo.
Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
15 Khona wonke amadoda ayesazi ukuthi omkabo batshisela abanye onkulunkulu impepha, labo bonke abesifazana ababemi khona, ixuku elikhulu, labo bonke abantu ababehlala elizweni leGibhithe, ePatrosi, bamphendula uJeremiya, besithi:
Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
16 Lelilizwi olikhulume kithi ebizweni leNkosi, kasiyikukulalela.
“Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
17 Kodwa sizakwenza lokwenza loba yiyiphi into ephume emlonyeni wethu, ukutshisela indlovukazi yamazulu impepha, siyithululele iminikelo yokunathwayo, njengoba besisenza, thina, labobaba, amakhosi ethu, leziphathamandla zethu, emizini yakoJuda lezitaladeni zeJerusalema; khona sasutha isinkwa, sasiphilile, kasibonanga okubi.
Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
18 Kodwa kusukela lapho sayekela ukutshisela indlovukazi yamazulu impepha lokuyithululela iminikelo yokunathwayo, siswele konke, siqedwe ngenkemba layindlala.
Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
19 Futhi lapho sitshisela indlovukazi yamazulu impepha, siyithululela iminikelo yokunathwayo, siyayenzela amakhekhe ngokwesifanekiso sayo, siyithululela iminikelo yokuthululwa, ngaphandle kwamadoda enu yini?
Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
20 UJeremiya wasekhuluma kubo bonke abantu, emadodaneni, lakwabesifazana, lakubo bonke abantu ababemphendule ngalelolizwi, esithi:
Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
21 Impepha elayitshisa emizini yakoJuda lezitaladeni zeJerusalema, lina, laboyihlo, amakhosi enu, leziphathamandla zenu, labantu belizwe, iNkosi kayiyikukukhumbula yini, kuvele enhliziyweni yayo?
“Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
22 Kwaze kwathi iNkosi yayingaselakukuthwala, ngenxa yobubi bezenzo zenu, ngenxa yezinengiso elazenzayo; ngakho ilizwe lenu laba yincithakalo lokwesabisayo lesiqalekiso, ukuze kungahlali muntu, njengalamuhla.
Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
23 Ngenxa yokuthi litshisile impepha, lokuthi lonile eNkosini, kalilalelanga ilizwi leNkosi, kalihambanga ngomlayo wayo langezimiso zayo langezifakazelo zayo; ngenxa yalokho okubi lokhu kwenzakele kini, njengalamuhla.
Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
24 UJeremiya wasesithi kubo bonke abantu lakwabesifazana bonke: Zwanini ilizwi leNkosi, wonke uJuda oselizweni leGibhithe.
Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
25 Itsho njalo iNkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli, ithi: Lina labomkenu, likhulumile ngomlomo wenu, lakugcwalisa ngezandla zenu, lisithi: Sizakwenza lokwenza izithembiso zethu esizithembisayo zokutshisela indlovukazi yamazulu impepha, lokuyithululela iminikelo yokunathwayo. Lizaqinisa lokuqinisa izithembiso zenu, lenze sibili izithembiso zenu!
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
26 Ngakho zwanini ilizwi leNkosi, lonke Juda elihlala elizweni leGibhithe: Khangelani, mina ngifungile ngebizo lami elikhulu, itsho iNkosi: Ibizo lami kalisayikubizwa ngumlomo waloba ngubani wakoJuda, elizweni lonke leGibhithe, esithi: Kuphila kweNkosi uJehova.
Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
27 Khangela, ngizabalindela ngokubi, kungeyisikho ngokuhle; lawo wonke amadoda akoJuda aselizweni leGibhithe azaqedwa ngenkemba layindlala, aze aphele.
Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
28 Lalabo abaphepha enkembeni bazabuyela elizweni lakoJuda bevela elizweni leGibhithe, balutshwana ngenani; layo yonke insali yakoJuda eze elizweni leGibhithe ukuhlala khona njengowezizwe, izakwazi ukuthi ilizwi elizakuma ngelikabani, elami kumbe elayo.
Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
29 Lalokhu kuzakuba yisibonakaliso kini, kutsho iNkosi, ukuthi ngizalijezisa kulindawo, ukuze lazi ukuthi amazwi ami azakuma lokuma emelana lani ngokubi.
“Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
30 Itsho njalo iNkosi: Khangelani, ngizanikela uFaro Hofira inkosi yeGibhithe esandleni sezitha zakhe, lesandleni salabo abadinga impilo yakhe, njengoba nganikela uZedekhiya inkosi yakoJuda esandleni sikaNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni, isitha sakhe, esadinga impilo yakhe.
Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”

< UJeremiya 44 >